< Yobu 42 >

1 Pamenepo Yobu anayankha Yehova kuti,
UJobe waseyiphendula iNkosi wathi:
2 “Ndikudziwa kuti Inu mungathe kuchita zinthu zonse; chimene mufuna kuchita wina sangaletse konse.
Ngiyazi ukuthi ungakwenza konke, lokuthi kakulacebo elingavinjelwa kuwe.
3 Munandifunsa kuti, ‘Kodi ndiwe yani amene ukufuna kusokoneza uphungu wanga ndi mawu opanda nzeru? Zoonadi ndinayankhula zimene sindinazimvetse, zinthu zodabwitsa kwambiri kwa ine zimene sindinazidziwe.
Ngubani lo ofiphaza iseluleko engelalwazi? Ngakho ngikhulumile lokho ebengingakuqedisisi, izinto ezimangalisayo kakhulu kimi, ebengingazazi.
4 “Inu munandiwuza kuti, ‘Mvetsetsa tsopano ndipo ndidzayankhula; ndidzakufunsa ndipo iwe udzandiyankhe.’
Ake uzwe, ngizakhuluma mina. Ngizakubuza, njalo wenze ngazi.
5 Ndinkangomva za Inu ndi makutu anga, koma tsopanonso ndakuonani ndi maso anga.
Ngokuzwa kwendlebe ngikuzwile, kodwa khathesi ilihlo lami liyakubona.
6 Nʼchifukwa chake ndi kuchita manyazi, ndikulapa podzithira fumbi ndi phulusa.”
Ngakho-ke ngiyazinenga, ngiyaphenduka ethulini lemlotheni.
7 Yehova atayankhula ndi Yobu mawu amenewa anawuza Elifazi wa ku Temani kuti, “Ine ndakukwiyira pamodzi ndi abwenzi ako awiri, chifukwa simunayankhule zabwino za Ine, monga mmene wayankhulira mtumiki wanga Yobu.
Kwasekusithi iNkosi isikhulume lamazwi kuJobe, iNkosi yathi kuElifazi umThemani: Ulaka lwami luyavutha kuwe lakubangane bakho ababili, ngoba kalikhulumanga ngami okuqondileyo njengenceku yami uJobe.
8 Kotero tsopano mutenge ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi kupita nazo kwa mtumiki wanga Yobu kuti mukapereke nsembe zopsereza. Mtumiki wanga Yobu adzakupemphererani, ndipo Ine ndidzalandira pemphero lake. Sindidzakuchitirani kanthu molingana ndi uchitsiru wanu. Inu simunayankhule zabwino za Ine, monga anayankhulira Yobu mtumiki wanga.”
Ngakho-ke zithatheleni amajongosi ayisikhombisa lenqama eziyisikhombisa, liye encekwini yami uJobe, lizinikelele umnikelo wokutshiswa, njalo uJobe inceku yami uzalikhulekela; ngoba isibili ngizakwemukela ubuso bakhe, ukuze ngingenzi kini njengobuthutha benu; ngoba kalikhulumanga ngami okuqondileyo njengenceku yami uJobe.
9 Motero Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama anachita zimene Yehova anawawuza ndipo Yehova anamvera pemphero la Yobu.
Ngakho bahamba oElifazi umThemani loBilidadi umShuhi loZofari umNahama, benza njengokutsho kweNkosi kubo; njalo iNkosi yemukela ubuso bukaJobe.
10 Yobu atawapempherera abwenzi ake aja, Yehova anamubwezera chuma chake ndipo anamupatsa mowirikiza kuposa zomwe anali nazo kale.
INkosi yasiphendula ukuthunjwa kukaJobe esekhulekele abangane bakhe; njalo iNkosi yengezelela konke uJobe ayelakho kuze kuphindwe kabili.
11 Abale ake ndi alongo ake onse, kuphatikizapo onse amene ankamudziwa kale, amabwera kwa iye nʼkudzadya naye chakudya mʼnyumba mwake. Iwo anamutonthoza ndi kumupepesa chifukwa cha mavuto onse amene Yehova analola kuti amugwere. Aliyense wa iwowa anamupatsa ndalama ndi mphete yagolide.
Kwasekufika kuye bonke abafowabo labo bonke odadewabo, labo bonke ababemazi mandulo, badla isinkwa laye endlini yakhe, bamkhalela, bamduduza ngakho konke okubi iNkosi eyayimehlisele khona; bamnika ngulowo lalowo uhlamvu lwemali, langulowo lalowo isongo legolide.
12 Yehova anadalitsa Yobu pa masiku ake otsirizawa kupambana poyamba paja. Iye anali ndi nkhosa 14,000, ngamira 6,000, ngʼombe zantchito 2,000 ndi abulu aakazi 1,000.
INkosi yasibusisa isiphetho sikaJobe okwedlula ukuqala kwakhe; ngoba waba lezimvu ezizinkulungwane ezilitshumi lane, lamakamela azinkulungwane eziyisithupha, lezipane zenkabi eziyinkulungwane, labobabhemi abasikazi abayinkulungwane.
13 Anaberekanso ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu.
Wasesiba lamadodana ayisikhombisa lamadodakazi amathathu.
14 Mwana wake wamkazi woyamba anamutcha Yemima, wachiwiri anamutcha Keziya, wachitatu anamutcha Kereni Hapuki.
Wasebiza ibizo leyokuqala wathi nguJemima, lebizo leyesibili wathi nguKeziya, lebizo leyesithathu wathi nguKereni-Hapuki.
15 Mʼdziko monsemo munalibe akazi okongola ngati ana a Yobu, ndipo abambo awo anawapatsa cholowa pamodzi ndi alongo awo.
Njalo kakutholakalanga abesifazana abahle njengamadodakazi kaJobe elizweni lonke; loyise wawanika ilifa phakathi kwabanewabo.
16 Zitachitika zimenezi, Yobu anakhala ndi moyo zaka 140. Iye anaona zidzukulu zake mpaka mʼbado wachinayi.
Lemva kwalokho uJobe waphila iminyaka elikhulu lamatshumi amane; wabona amadodana akhe, lamadodana amadodana akhe, kwaze kwaba yizizukulwana ezine.
17 Potsiriza, Yobu anamwalira ali nkhalamba ya zaka zochuluka kwambiri.
UJobe wasesifa, emdala, enele ngezinsuku.

< Yobu 42 >