< Yobu 42 >

1 Pamenepo Yobu anayankha Yehova kuti,
Så svarede Job HERREN og sagde:
2 “Ndikudziwa kuti Inu mungathe kuchita zinthu zonse; chimene mufuna kuchita wina sangaletse konse.
"Jeg ved, at du magter alt, for dig er intet umuligt!
3 Munandifunsa kuti, ‘Kodi ndiwe yani amene ukufuna kusokoneza uphungu wanga ndi mawu opanda nzeru? Zoonadi ndinayankhula zimene sindinazimvetse, zinthu zodabwitsa kwambiri kwa ine zimene sindinazidziwe.
"Hvem fordunkler mit Råd med Ord, som er uden Indsigt?" Derfor: jeg talte uden Forstand om noget, som var mig for underfuldt, og som jeg ej kendte til.
4 “Inu munandiwuza kuti, ‘Mvetsetsa tsopano ndipo ndidzayankhula; ndidzakufunsa ndipo iwe udzandiyankhe.’
Hør dog, og jeg vil tale, jeg vil spørge, og du skal lære mig!
5 Ndinkangomva za Inu ndi makutu anga, koma tsopanonso ndakuonani ndi maso anga.
Jeg havde kun hørt et Rygte om dig, men nu har mit Øje set dig;
6 Nʼchifukwa chake ndi kuchita manyazi, ndikulapa podzithira fumbi ndi phulusa.”
jeg tager det derfor tilbage og angrer i Støv og Aske!
7 Yehova atayankhula ndi Yobu mawu amenewa anawuza Elifazi wa ku Temani kuti, “Ine ndakukwiyira pamodzi ndi abwenzi ako awiri, chifukwa simunayankhule zabwino za Ine, monga mmene wayankhulira mtumiki wanga Yobu.
Men efter at HERREN havde talet disse Ord til Job, sagde han til Temaniten Elifaz: "Min Vrede er blusset op mod dig og dine to Venner, fordi I ikke talte rettelig om mig som min Tjener Job!
8 Kotero tsopano mutenge ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi kupita nazo kwa mtumiki wanga Yobu kuti mukapereke nsembe zopsereza. Mtumiki wanga Yobu adzakupemphererani, ndipo Ine ndidzalandira pemphero lake. Sindidzakuchitirani kanthu molingana ndi uchitsiru wanu. Inu simunayankhule zabwino za Ine, monga anayankhulira Yobu mtumiki wanga.”
Tag eder derfor syv Tyre og syv Vædre og gå til min Tjener Job og bring et Brændoffer for eder. Og min Tjener Job skal gå i Forbøn for eder, thi ham vil jeg bønhøre, så jeg ikke gør en Ulykke på eder, fordi I ikke talte rettelig om mig som min Tjener Job!"
9 Motero Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama anachita zimene Yehova anawawuza ndipo Yehova anamvera pemphero la Yobu.
Så gik Temaniten Elifaz, Sjuhiten Bildad og Na'amatiten Zofar hen og gjorde, som HERREN havde sagt, og HERREN bønhørte Job.
10 Yobu atawapempherera abwenzi ake aja, Yehova anamubwezera chuma chake ndipo anamupatsa mowirikiza kuposa zomwe anali nazo kale.
Og HERREN vendte Jobs Skæbne, da han gik i Forbøn for sine Venner; og HERREN gav Job alt, hvad han havde ejet, tvefold igen.
11 Abale ake ndi alongo ake onse, kuphatikizapo onse amene ankamudziwa kale, amabwera kwa iye nʼkudzadya naye chakudya mʼnyumba mwake. Iwo anamutonthoza ndi kumupepesa chifukwa cha mavuto onse amene Yehova analola kuti amugwere. Aliyense wa iwowa anamupatsa ndalama ndi mphete yagolide.
Så kom alle hans Brødre og Søstre og alle, der kendte ham tilforn, og holdt Måltid med ham i hans Hus, og de viste ham deres Medfølelse og trøstede ham over al den Ulykke, HERREN havde bragt over ham, og de gav ham hver en Kesita og en Guldring.
12 Yehova anadalitsa Yobu pa masiku ake otsirizawa kupambana poyamba paja. Iye anali ndi nkhosa 14,000, ngamira 6,000, ngʼombe zantchito 2,000 ndi abulu aakazi 1,000.
Og HERREN velsignede Jobs sidste Tid mere end hans første. Han fk 14000 Stykker Småkvæg, og 1000 Aseninder.
13 Anaberekanso ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu.
Og han fik syv Sønner og tre Døtre,
14 Mwana wake wamkazi woyamba anamutcha Yemima, wachiwiri anamutcha Keziya, wachitatu anamutcha Kereni Hapuki.
og han kaldte den ene Jemima, den anden Kezia og den tredje Keren-Happuk.
15 Mʼdziko monsemo munalibe akazi okongola ngati ana a Yobu, ndipo abambo awo anawapatsa cholowa pamodzi ndi alongo awo.
Så smukke Kvinder som Jobs Døtre fandtes ingensteds på Jorden; og deres Fader gav dem Arv imellem deres Brødre:
16 Zitachitika zimenezi, Yobu anakhala ndi moyo zaka 140. Iye anaona zidzukulu zake mpaka mʼbado wachinayi.
Siden levede Job 140 År og så sine Børn og Børnebørn, fire Slægtled.
17 Potsiriza, Yobu anamwalira ali nkhalamba ya zaka zochuluka kwambiri.
Så døde Job gammel og mæt af Dage.

< Yobu 42 >