< Yobu 42 >

1 Pamenepo Yobu anayankha Yehova kuti,
Da svarede Job Herren og sagde:
2 “Ndikudziwa kuti Inu mungathe kuchita zinthu zonse; chimene mufuna kuchita wina sangaletse konse.
Jeg ved, at du formaar alting, og at ingen Tanke er dig forment.
3 Munandifunsa kuti, ‘Kodi ndiwe yani amene ukufuna kusokoneza uphungu wanga ndi mawu opanda nzeru? Zoonadi ndinayankhula zimene sindinazimvetse, zinthu zodabwitsa kwambiri kwa ine zimene sindinazidziwe.
„Hvo er den, som fordunkler Guds Raad uden Forstand”? — Saa har jeg udtalt mig om det, som jeg ikke forstod, om de Ting, som vare mig for underlige, hvilke jeg ikke kendte.
4 “Inu munandiwuza kuti, ‘Mvetsetsa tsopano ndipo ndidzayankhula; ndidzakufunsa ndipo iwe udzandiyankhe.’
Hør dog, og jeg vil tale; jeg vil spørge dig, og undervis du mig!
5 Ndinkangomva za Inu ndi makutu anga, koma tsopanonso ndakuonani ndi maso anga.
Jeg havde hørt om dig af Rygte, men nu har mit Øje set dig.
6 Nʼchifukwa chake ndi kuchita manyazi, ndikulapa podzithira fumbi ndi phulusa.”
Derfor forkaster jeg, hvad jeg har sagt, og angrer i Støv og Aske.
7 Yehova atayankhula ndi Yobu mawu amenewa anawuza Elifazi wa ku Temani kuti, “Ine ndakukwiyira pamodzi ndi abwenzi ako awiri, chifukwa simunayankhule zabwino za Ine, monga mmene wayankhulira mtumiki wanga Yobu.
Og det skete, efter at Herren havde talt disse Ord til Job, da sagde Herren til Elifas, Themaniten: Min Vrede er optændt imod dig og imod dine to Venner; thi I have ikke talt ret om mig, saaledes som min Tjener Job.
8 Kotero tsopano mutenge ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi kupita nazo kwa mtumiki wanga Yobu kuti mukapereke nsembe zopsereza. Mtumiki wanga Yobu adzakupemphererani, ndipo Ine ndidzalandira pemphero lake. Sindidzakuchitirani kanthu molingana ndi uchitsiru wanu. Inu simunayankhule zabwino za Ine, monga anayankhulira Yobu mtumiki wanga.”
Saa tager eder nu syv Tyre og syv Vædre, og gaar til min Tjener Job, og ofrer Brændoffer for eder, og Job, min Tjener, skal bede for eder; ikkun hans Person vil jeg anse, at jeg ikke skal lade eders Daarlighed gaa ud over eder; thi I have ikke talt ret om mig, saaledes som min Tjener Job.
9 Motero Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama anachita zimene Yehova anawawuza ndipo Yehova anamvera pemphero la Yobu.
Saa gik Elifas Themaniten og Bildad Sukiten og Zofar Naamathiten, og de gjorde, ligesom Herren havde sagt til dem; og Herren ansaa Jobs Person.
10 Yobu atawapempherera abwenzi ake aja, Yehova anamubwezera chuma chake ndipo anamupatsa mowirikiza kuposa zomwe anali nazo kale.
Og Herren vendte Jobs Fangenskab, der han havde bedet for sine Venner; og Herren forøgede alt det, Job havde haft, til det dobbelte.
11 Abale ake ndi alongo ake onse, kuphatikizapo onse amene ankamudziwa kale, amabwera kwa iye nʼkudzadya naye chakudya mʼnyumba mwake. Iwo anamutonthoza ndi kumupepesa chifukwa cha mavuto onse amene Yehova analola kuti amugwere. Aliyense wa iwowa anamupatsa ndalama ndi mphete yagolide.
Og alle hans Brødre og alle hans Søstre og alle, som kendte ham tilforn, kom til ham og aade Brød med ham i hans Hus og viste ham Deltagelse og trøstede ham over alt det onde, som Herren havde ladet komme over ham; og de gave ham hver en Penning og hver et Smykke af Guld.
12 Yehova anadalitsa Yobu pa masiku ake otsirizawa kupambana poyamba paja. Iye anali ndi nkhosa 14,000, ngamira 6,000, ngʼombe zantchito 2,000 ndi abulu aakazi 1,000.
Og Herren velsignede Jobs sidste Levetid fremfor den første; og han fik fjorten Tusinde Faar og seks Tusinde Kameler og tusinde Par Øksne og tusinde Aseninder.
13 Anaberekanso ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu.
Og han fik syv Sønner og tre Døtre.
14 Mwana wake wamkazi woyamba anamutcha Yemima, wachiwiri anamutcha Keziya, wachitatu anamutcha Kereni Hapuki.
Og han kaldte den førstes Navn Jemima og den andens Navn Kezia og den tredjes Navn Keren-Happuk.
15 Mʼdziko monsemo munalibe akazi okongola ngati ana a Yobu, ndipo abambo awo anawapatsa cholowa pamodzi ndi alongo awo.
Og der blev ikke fundet saa dejlige Kvinder som Jobs Døtre i hele Landet, og deres Fader gav dem Arv iblandt deres Brødre.
16 Zitachitika zimenezi, Yobu anakhala ndi moyo zaka 140. Iye anaona zidzukulu zake mpaka mʼbado wachinayi.
Og Job levede derefter hundrede og fyrretyve Aar og saa sine Børn og sine Børnebørn i fjerde Slægt.
17 Potsiriza, Yobu anamwalira ali nkhalamba ya zaka zochuluka kwambiri.
Og Job døde, gammel og mæt af Dage.

< Yobu 42 >