< Yobu 41 >
1 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
“Livyatan'ı çengelle çekebilir misin, Dilini halatla bağlayabilir misin?
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
Burnuna sazdan ip takabilir misin, Kancayla çenesini delebilir misin?
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
Yalvarıp yakarır mı sana, Tatlı tatlı konuşur mu?
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
Seninle antlaşma yapar mı, Onu ömür boyu köle edesin diye?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
Kuşla oynar gibi onunla oynayabilir misin, Hizmetçilerin eğlensin diye ona tasma takabilir misin?
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
Balıkçılar onun üzerine pazarlık eder mi? Tüccarlar aralarında onu böler mi?
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
Derisini zıpkınlarla, Başını mızraklarla doldurabilir misin?
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
Elini üzerine koy da, çıkacak çıngarı gör, Bir daha yapmayacaksın bunu.
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
Onu yakalamak için umutlanma, Görünüşü bile insanın ödünü patlatır.
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
Onu uyandıracak kadar yürekli adam yoktur. Öyleyse benim karşımda kim durabilir?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
Kim benden hesap vermemi isteyebilir? Göklerin altında ne varsa bana aittir.
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
“Onun kolları, bacakları, Zorlu gücü, güzel yapısı hakkında Konuşmadan edemeyeceğim.
13 Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
Onun giysisinin önünü kim açabilir? Kim onun iki katlı zırhını delebilir?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
Ağzının kapılarını açmaya kim yeltenebilir, Dehşet verici dişleri karşısında?
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
Sımsıkı kenetlenmiştir Sırtındaki sıra sıra pullar,
16 Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
Öyle yakındır ki birbirine Aralarından hava bile geçmez.
17 Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
Birbirlerine geçmişler, Yapışmış, ayrılmazlar.
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
Aksırması ışık saçar, Gözleri şafak gibi parıldar.
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
Ağzından alevler fışkırır, Kıvılcımlar saçılır.
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
Kaynayan kazandan, Yanan sazdan çıkan duman gibi Burnundan duman tüter.
21 Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
Soluğu kömürleri tutuşturur, Alev çıkar ağzından.
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
Boynu güçlüdür, Dehşet önü sıra gider.
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
Etinin katmerleri birbirine yapışmış, Sertleşmiş üzerinde, kımıldamazlar.
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
Göğsü taş gibi serttir, Değirmenin alt taşı gibi sert.
25 Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
Ayağa kalktı mı güçlüler dehşete düşer, Çıkardığı gürültüden ödleri patlar.
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
Üzerine gidildi mi ne kılıç işler, Ne mızrak, ne cirit, ne de kargı.
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
Demir saman gibi gelir ona, Tunç çürük odun gibi.
28 Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
Oklar onu kaçırmaz, Anız gibi gelir ona sapan taşları.
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
Anız sayılır onun için topuzlar, Vınlayan palaya güler.
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
Keskin çömlek parçaları gibidir karnının altı, Düven gibi uzanır çamura.
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
Derin suları kaynayan kazan gibi fokurdatır, Denizi merhem çömleği gibi karıştırır.
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
Ardında parlak bir iz bırakır, İnsan enginin saçları ağarmış sanır.
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
Yeryüzünde bir eşi daha yoktur, Korkusuz bir yaratıktır.
34 Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
Kendini büyük gören her varlığı aşağılar, Gururlu her varlığın kralı odur.”