< Yobu 41 >
1 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
¿Es posible sacar al Leviatán con un anzuelo, o poner un anzuelo en su boca?
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
¿Le pondrás un cordón en la nariz o le perforarás con un gancho su quijada?
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
¿Te hará oraciones o te hará súplicas?
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
¿Hará acuerdo contigo para que lo tomes por siervo para siempre?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
¿Jugarás con él, como con un pájaro? ¿O lo ataras para tus doncellas?
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
¿Le sacarán provecho los pescadores? ¿Lo cortarán en pedazos los comerciantes?
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
¿Pondrás atravesar con flechas de hierro de punta afilada en su piel, o su cabeza con arpones?
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
Solo pon tu mano sobre él, y mira qué pelea tendrás; ¡No lo volverás a hacer!
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
En verdad, la esperanza de su atacante es falsa; Él es vencido incluso al verlo!
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
Es tan cruel que nadie está dispuesto a ir contra él. ¿Quién es capaz de mantener su lugar delante de mí?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
¿Quién me ha confrontado para que yo le restituya? Cuanto existe debajo del cielo es mío.
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
No guardaré silencio sobre las partes de su cuerpo, o sobre su poder y la fuerza de su cuerpo.
13 Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
¿Quién le ha quitado su piel exterior? ¿Quién puede entrar dentro de su doble coraza?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
¿Quién ha abierto las puertas de su rostro? La hilera de sus dientes espantan.
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
Su fuerte espalda de escamas es su orgullo, unidas entre sí, una contra la otra, como un sello.
16 Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
Uno está tan cerca del otro que ningún aire puede interponerse entre ellos.
17 Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
Se agarran el uno al otro; se juntan, para que no se puedan separar.
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
Sus estornudos emiten llamas, y sus ojos son como los de la aurora.
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
De su boca salen las luces encendidas, y las llamas de fuego saltan.
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
De su nariz sale humo, como una olla hirviendo sobre el fuego.
21 Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
Su aliento pone fuego a las brasas, y una llama sale de su boca.
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
La fuerza está en su cuello, y el desaliento danza ante él.
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
Los pliegues de su piel están unidas, fijas y no para ser movidas.
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
Su corazón es tan fuerte como una piedra, duro como la piedra trituradora de abajo.
25 Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
Cuando se levanta él, los poderosos son vencidos por el miedo, por quebrantamiento del pecado.
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
La espada puede acercarse a él, pero no puede atravesarlo; la lanza, o la flecha, o el hierro afilado.
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
El hierro es para él como hierba seca, y el bronce como madera blanda.
28 Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
La flecha no puede ponerlo en vuelo: las piedras no son más que paja para él.
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
Un palo grueso no es mejor que una hoja de hierba, y él se burla con el ataque de la lanza.
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
Debajo de él hay bordes afilados de macetas rotas: como si estuviera tirando de trillos sobre él lodo.
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
Lo profundo de la mar está hirviendo como una olla de especias, y el mar como una vasija de perfume.
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
Después de él, su camino brilla, de modo que lo profundo parece una cabellera blanca.
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
En la tierra no hay otro como él, que está hecho sin miedo.
34 Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
Todo ser altivo lo desafía; Él es rey sobre todos los hijos de orgullo.