< Yobu 41 >
1 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
“¿Puedes sacar al Leviatán con un anzuelo? o presionar su lengua con una cuerda?
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
¿Puedes poner una cuerda en su nariz, o atravesar su mandíbula con un gancho?
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
Te hará muchas peticiones, ¿o te hablará con palabras suaves?
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
Hará un pacto con vosotros, para que lo tomes por siervo para siempre?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
¿Jugarás con él como con un pájaro? ¿O lo atarás para tus chicas?
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
¿Los comerciantes harán un trueque por él? ¿Lo repartirán entre los comerciantes?
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
Puede llenar su piel con hierros de púas, o su cabeza con lanzas de pescado?
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
Pon tu mano sobre él. Recuerda la batalla, y no lo hagas más.
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
He aquí que la esperanza de él es vana. ¿No se abatirá uno incluso al verlo?
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
Nadie es tan feroz que se atreva a agitarlo. ¿Quién es, pues, el que puede presentarse ante mí?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
¿Quién me ha dado primero, para que yo le pague? Todo bajo el cielo es mío.
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
“No guardaré silencio sobre sus miembros, ni su poderosa fuerza, ni su buena contextura.
13 Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
¿Quién puede despojarse de su prenda exterior? ¿Quién se acercará a sus fauces?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
¿Quién puede abrir las puertas de su rostro? Alrededor de sus dientes está el terror.
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
Las fuertes escamas son su orgullo, encerrados juntos con un cierre hermético.
16 Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
Uno está tan cerca de otro, que ningún aire pueda interponerse entre ellos.
17 Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
Están unidos entre sí. Se pegan entre sí, de modo que no se pueden separar.
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
Su estornudo hace brillar la luz. Sus ojos son como los párpados de la mañana.
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
De su boca salen antorchas ardientes. Saltan chispas de fuego.
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
De sus fosas nasales sale un humo, como de una olla hirviendo sobre un fuego de cañas.
21 Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
Su aliento enciende las brasas. Una llama sale de su boca.
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
Hay fuerza en su cuello. El terror baila ante él.
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
Las escamas de su carne están unidas. Son firmes con él. No se pueden mover.
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
Su corazón es firme como una piedra, sí, firme como la piedra de molino inferior.
25 Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
Cuando se levanta, los poderosos tienen miedo. Se retiran ante su paliza.
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
Si uno lo ataca con la espada, no puede prevalecer; ni la lanza, ni el dardo, ni el asta puntiaguda.
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
Cuenta el hierro como paja, y el bronce como la madera podrida.
28 Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
La flecha no puede hacerle huir. Las piedras de la honda son como la paja para él.
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
Los palos se cuentan como rastrojos. Se ríe de las prisas de la jabalina.
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
Sus partes inferiores son como alfareros afilados, dejando un rastro en el barro como un trineo.
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
Hace que lo profundo hierva como una olla. Hace que el mar sea como un bote de pomada.
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
Hace brillar un camino tras él. Se diría que el profundo tiene el pelo blanco.
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
En la tierra no hay nada igual, que se hace sin miedo.
34 Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
Él ve todo lo que es alto. Es el rey de todos los hijos de la soberbia”.