< Yobu 41 >

1 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
Поць ту сэ принзь левиатанул ку ундица сау сэ-й леӂь лимба ку о фуние?
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
Ый вей путя петрече папура прин нэрь сау сэ-й стрэпунӂь ку ун кырлиг фалка?
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
Ыць ва фаче ел мулте ругэминць? Ыць ва ворби ел ку ун глас дулче?
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
Ва фаче ел ун легэмынт ку тине, ка сэ-ць фие роб пе вечие?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
Те вей жука ту ку ел ка ши ку о пасэре? Ыл вей лега ту ка сэ-ць ынвеселешть фетеле?
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
Фак пескарий негоц ку ел? Ыл ымпарт ей ынтре негусторь?
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
Ый вей акопери пеля ку цепуше ши капул ку кинӂь?
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
Ридикэ-ць нумай мына ымпотрива луй, ши ну-ць ва май вени густ сэ-л ловешть.
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
Ятэ кэ ешть ыншелат ын аштептаря та де а-л принде: нумай сэ-л везь, ши казь ла пэмынт!
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
Нимень ну есте атыт де ындрэзнец ка сэ-л ынтэрыте. Чине Ми с-ар ымпотриви ын фацэ?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
Куй сунт датор, ка сэ-й плэтеск? Суб чер тотул есте ал Меу.
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
Вряу сэ май ворбеск ярэшь де мэдулареле луй ши де тэрия луй, ши де фрумусеця ынтокмирий луй.
13 Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
Чине-й ва путя ридика вешмынтул? Чине ва путя пэтрунде ынтре фэлчиле луй?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
Чине ва путя дескиде порциле гурий луй? Шируриле динцилор луй кыт сунт де ынспэймынтэтоаре!
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
Скутуриле луй мэреце ши путерниче сунт уните ымпреунэ ка принтр-о печете;
16 Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
се цин унул де алтул ши нич аерул н-ар путя трече принтре еле.
17 Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
Сунт ка ниште фраць каре се ымбрэцишязэ, се апукэ ши рэмын недеспэрциць.
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
Стрэнутуриле луй фак сэ стрэлучяскэ лумина; окий луй сунт ка ӂяна зорилор.
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
Дин гура луй цышнеск флэкэрь, скапэрэ скынтей де фок дин еа.
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
Дин нэриле луй есе фум, ка динтр-ун вас каре фербе, ка динтр-о кэлдаре фербинте.
21 Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
Суфларя луй апринде кэрбуний ши гура луй арункэ флэкэрь.
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
Тэрия луй стэ ын грумаз ши ынаинтя луй саре гроаза.
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
Пэрциле луй челе кэрноасе се цин ымпреунэ, ка турнате пе ел, неклинтите.
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
Инима луй есте таре ка пятра, таре ка пятра де моарэ каре стэ дедесубт.
25 Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
Кынд се скоалэ ел, тремурэ витежий ши спайма ый пуне пе фугэ.
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
Деӂяба есте ловит ку сабия; кэч сулица, сэӂята ши павэза ну фолосеск ла нимик.
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
Пентру ел, ферул есте ка паюл, арама, ка лемнул путред.
28 Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
Сэӂята ну-л пуне пе фугэ, петреле дин праштие сунт ка плява пентру ел.
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
Ну веде ын гьоагэ декыт ун фир де пай ши рыде ла шуератул сэӂецилор.
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
Суб пынтечеле луй сунт цепь аскуциць: ай зиче кэ есте о грапэ ынтинсэ песте норой.
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
Фаче сэ клокотяскэ фундул мэрий ка ун казан ши-л клатинэ ка пе ун вас плин ку мир.
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
Ын урмэ, ел ласэ о кэраре луминоасэ, ши адынкул паре ка плетеле унуй бэтрын.
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
Пе пэмынт нимик ну-й есте стэпын; есте фэкут ка сэ ну се тямэ де нимик.
34 Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
Привеште ку диспрец тот че есте ынэлцат, есте ымпэратул челор май мындре добитоаче.”

< Yobu 41 >