< Yobu 41 >
1 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
Poderás tu pescar ao leviatã com anzol, ou abaixar sua língua com uma corda?
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
Podes pôr um anzol em seu nariz, ou com um espinho furar sua queixada?
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
Fará ele súplicas a ti, [ou] falará contigo suavemente?
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
Fará ele pacto contigo, para que tu o tomes por escravo perpétuo?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
Brincarás tu com ele como com um passarinho, ou o atarás para tuas meninas?
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
Os companheiros farão banquete dele? Repartirão dele entre os mercadores?
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
Poderás tu encher sua pele de espetos, ou sua cabeça com arpões de pescadores?
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
Põe tua mão sobre ele; te lembrarás da batalha, e nunca mais voltarás a fazer.
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
Eis que a esperança de alguém [de vencê-lo] falhará; pois, apenas ao vê-lo será derrubado.
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
Ninguém há [tão] ousado que o desperte; quem pois, [ousa] se opor a mim?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
Quem me deu primeiro, para que eu [o] recompense? Tudo o que há debaixo dos céus é meu.
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
Eu não me calarei a respeito de seus membros, nem de [suas] forças, e da graça de sua estatura.
13 Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
Quem descobrirá sua vestimenta superficial? Quem poderá penetrar sua couraça dupla?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
Quem poderia abrir as portas de seu rosto? Ao redor de seus dentes há espanto.
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
Seus fortes escudos são excelentes; cada um fechado, como um selo apertado.
16 Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
Um está tão próximo do outro, que vento não pode entrar entre eles.
17 Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
Estão grudados uns aos outros; estão tão travados entre si, que não se podem separar.
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
Cada um de seus roncos faz resplandecer a luz, e seus olhos são como os cílios do amanhecer.
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
De sua boca saem tochas, faíscas de fogo saltam dela.
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
De suas narinas sai fumaça, como de uma panela fervente ou de um caldeirão.
21 Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
Seu fôlego acende carvões, e de sua boca sai chama.
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
A força habita em seu pescoço; diante dele salta-se de medo.
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
As dobras de sua carne estão apegadas [entre si]; cada uma está firme nele, e não podem ser movidas.
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
Seu coração é rígido como uma pedra, rígido como a pedra de baixo de um moinho.
25 Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
Quando ele se levanta, os fortes tremem; por [seus] abalos se recuam.
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
Se alguém lhe tocar com a espada, não poderá prevalecer; nem arremessar dardo, ou lança.
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
Ele considera o ferro como palha, e o aço como madeira podre.
28 Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
A flecha não o faz fugir; as pedras de funda são para ele como sobras de cascas.
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
Considera toda arma como sobras de cascas, e zomba do mover da lança.
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
Por debaixo de si tem conchas pontiagudas; ele esmaga com suas pontas na lama.
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
Ele faz ferver as profundezas como a uma panela, e faz do mar como um pote de unguento.
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
Ele faz brilhar o caminho atrás de si; faz parecer ao abismo com cabelos grisalhos.
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
Não há sobre a terra algo que se possa comparar a ele. Ele foi feito para não temer.
34 Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
Ele vê tudo que é alto; ele é rei sobre todos os filhos dos animais soberbos.