< Yobu 41 >

1 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
Kan du dra Leviatan op med en krok og trykke dens tunge ned med et snøre?
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
Kan du sette en sivline i dens nese og gjennembore dens kjeve med en krok?
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
Vil den rette mange ydmyke bønner til dig eller tale blide ord til dig?
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
Vil den gjøre en pakt med dig, så du kan få den til din træl for all tid?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
Kan du leke med den som med en fugl og binde den fast for dine små piker?
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
Kan et lag av fiskere kjøpslå om den, stykke den ut mellem kjøbmennene?
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
Kan du fylle dens hud med spyd og dens hode med harpuner?
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
Prøv å legge hånd på den! Den strid skal du komme til å minnes og ikke gjøre det igjen!
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
Nei, den som våger slikt, hans håp blir sveket; allerede ved synet av den styrter han til jorden.
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
Ingen er så djerv at han tør tirre den; hvem tør da sette sig op imot mig?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
Hvem gav mig noget først, så jeg skulde gi ham vederlag? Alt under himmelen hører mig til.
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
Jeg vil ikke tie om dens lemmer, om dens store styrke og dens fagre bygning.
13 Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
Hvem har dradd dens klædning av? Hvem tør komme innenfor dens dobbelte rad av tenner?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
Hvem har åpnet dens kjevers dør? Rundt om dens tenner er redsel.
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
Stolte er skjoldenes rader; hvert av dem er tillukket som med et fast segl.
16 Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
De ligger tett innpå hverandre, og ingen luft trenger inn imellem dem.
17 Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
Det ene skjold henger fast ved det andre; de griper inn i hverandre og skilles ikke at.
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
Når den nyser, stråler det frem lys, og dens øine er som morgenrødens øielokk.
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
Bluss farer ut av dens gap, gnister spruter frem.
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
Fra dens nesebor kommer røk som av en gryte som koker over siv.
21 Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
Dens ånde tender kull i brand, og luer går ut av dens gap.
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
På dens hals har styrken sin bolig, og angsten springer foran den.
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
Dens doglapper sitter fast; de er som støpt på den og rører sig ikke.
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
Dens hjerte er fast som sten, fast som den underste kvernsten.
25 Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
Når den hever sig, gruer helter; av redsel mister de sans og samling.
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
Rammes den med sverd, så biter det ikke på den, heller ikke lanse, pil eller kastespyd.
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
Den akter jern som strå, kobber som ormstukket tre.
28 Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
Buens sønn jager den ikke på flukt; slyngens stener blir som halm for den.
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
Stridsklubber aktes som halm, og den ler av det susende spyd.
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
På dens buk sitter skarpe skår, den gjør spor i dyndet som efter en treskeslede.
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
Den får dypet til å koke som en gryte; den får havet til å skumme som en salvekokers kjele.
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
Efter den lyser dens sti; dypet synes å ha sølvhår.
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
Det er intet på jorden som er herre over den; den er skapt til ikke å reddes.
34 Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
Alt som er høit, ser den i øiet; den er en konge over alle stolte dyr.

< Yobu 41 >