< Yobu 41 >

1 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
An extrahere poteris leviathan hamo, et fune ligabis linguam eius?
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
Numquid pones circulum in naribus eius, aut armilla perforabis maxillam eius?
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
Numquid multiplicabit ad te preces, aut loquetur tibi mollia?
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
Numquid feriet tecum pactum, et accipies eum servum sempiternum?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
Numquid illudes ei quasi avi, aut ligabis eum ancillis tuis?
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
Concident eum amici, divident illum negotiatores?
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
Numquid implebis sagenas pelle eius, et gurgustium piscium capite illius?
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
Pone super eum manum tuam: memento belli, nec ultra addas loqui.
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
Ecce, spes eius frustrabitur eum, et videntibus cunctis præcipitabitur.
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
Non quasi crudelis suscitabo eum: quis enim resistere potest vultui meo?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
Quis ante dedit mihi, ut reddam ei? omnia quæ sub cælo sunt, mea sunt.
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
Non parcam ei, et verbis potentibus, et ad deprecandum compositis.
13 Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
Quis revelabit faciem indumenti eius? et in medium oris eius quis intrabit?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
Portas vultus eius quis aperiet? per gyrum dentium eius formido.
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
Corpus illius quasi scuta fusilia, compactum squamis se prementibus.
16 Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
Una uni coniungitur, et ne spiraculum quidem incedit per eas:
17 Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
Una alteri adhærebit, et tenentes se nequaquam separabuntur.
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
Sternutatio eius splendor ignis, et oculi eius, ut palpebræ diluculi.
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
De ore eius lampades procedunt, sicut tædæ ignis accensæ.
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
De naribus eius procedit fumus, sicut ollæ succensæ atque ferventis.
21 Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
Halitus eius prunas ardere facit, et flamma de ore eius egreditur.
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
In collo eius morabitur fortitudo, et faciem eius præcedit egestas.
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
Membra carnium eius cohærentia sibi: mittet contra eum fulmina, et ad locum alium non ferentur.
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
Cor eius indurabitur tamquam lapis, et stringetur quasi malleatoris incus.
25 Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
Cum sublatus fuerit, timebunt angeli, et territi purgabuntur.
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
Cum apprehenderit eum gladius, subsitere non poterit neque hasta, neque thorax:
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
Reputabit enim quasi paleas ferrum, et quasi lignum putridum, æs.
28 Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
Non fugabit eum vir sagittarius, in stipulam versi sunt ei lapides fundæ.
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
Quasi stipulam æstimabit malleum, et deridebit vibrantem hastam.
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
Sub ipso erunt radii solis, et sternet sibi aurum quasi lutum.
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
Fervescere faciet quasi ollam profundum mare, et ponet quasi cum unguenta bulliunt.
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
Post eum lucebit semita, æstimabit abyssum quasi senescentem.
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
Non est super terram potestas, quæ comparetur ei, qui factus est ut nullum timeret.
34 Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
Omne sublime videt, ipse est rex super universos filios superbiæ.

< Yobu 41 >