< Yobu 41 >
1 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
Prenderai tu il coccodrillo all’amo? Gli assicurerai la lingua colla corda?
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
Gli passerai un giunco per le narici? Gli forerai le mascelle con l’uncino?
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
Ti rivolgerà egli molte supplicazioni? Ti dirà egli delle parole dolci?
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
Farà egli teco un patto perché tu lo prenda per sempre al tuo servizio?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
Scherzerai tu con lui come fosse un uccello? L’attaccherai a un filo per divertir le tue ragazze?
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
Ne trafficheranno forse i pescatori? Lo spartiranno essi fra i negozianti?
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
Gli coprirai tu la pelle di dardi e la testa di ramponi?
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
Mettigli un po’ le mani addosso!… Ti ricorderai del combattimento e non ci tornerai!
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
Ecco, fallace è la speranza di chi l’assale; basta scorgerlo e s’è atterrati.
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
Nessuno è tanto ardito da provocarlo. E chi dunque oserà starmi a fronte?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
Chi mi ha anticipato alcun che perch’io glielo debba rendere? Sotto tutti i cieli, ogni cosa è mia.
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
E non vo’ tacer delle sue membra, della sua gran forza, della bellezza della sua armatura.
13 Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
Chi l’ha mai spogliato della sua corazza? Chi è penetrato fra la doppia fila de’ suoi denti?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
Chi gli ha aperti i due battenti della gola? Intorno alla chiostra de’ suoi denti sta il terrore.
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
Superbe son le file de’ suoi scudi, strettamente uniti come da un sigillo.
16 Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
Uno tocca l’altro, e tra loro non passa l’aria.
17 Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
Sono saldati assieme, si tengono stretti, sono inseparabili.
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
I suoi starnuti dànno sprazzi di luce; i suoi occhi son come le palpebre dell’aurora.
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
Dalla sua bocca partono vampe, ne scappan fuori scintille di fuoco.
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
Dalle sue narici esce un fumo, come da una pignatta che bolla o da una caldaia.
21 Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
L’alito suo accende i carboni, e una fiamma gli erompe dalla gola.
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
Nel suo collo risiede la forza, dinanzi a lui salta il terrore.
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
Compatte sono in lui le parti flosce della carne, gli stanno salde addosso, non si muovono.
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
Il suo cuore è duro come il sasso, duro come la macina di sotto.
25 Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
Quando si rizza, tremano i più forti, e dalla paura son fuori di sé.
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
Invano lo si attacca con la spada; a nulla valgon lancia, giavellotto, corazza.
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
Il ferro è per lui come paglia; il rame, come legno tarlato.
28 Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
La figlia dell’arco non lo mette in fuga; le pietre della fionda si mutano per lui in stoppia.
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
Stoppia gli par la mazza e si ride del fremer della lancia.
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
Il suo ventre è armato di punte acute, e lascia come tracce d’erpice sul fango.
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
Fa bollire l’abisso come una caldaia, del mare fa come un gran vaso da profumi.
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
Si lascia dietro una scia di luce; l’abisso par coperto di bianca chioma.
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
Non v’è sulla terra chi lo domi; è stato fatto per non aver paura.
34 Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
Guarda in faccia tutto ciò ch’è eccelso, è re su tutte le belve più superbe”.