< Yobu 41 >

1 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
Can you draw out the leviathan with a hook, and can you bind his tongue with a cord?
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
Can you place a ring in his nose, or bore through his jaw with an arm band?
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
Will he offer many prayers to you, or speak to you quietly?
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
Will he form a covenant with you, and will you accept him as a servant forever?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
Will you play with him as with a bird, or tether him for your handmaids?
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
Will your friends cut him into pieces, will dealers distribute him?
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
Will you fill up bags with his hide, and let his head be used as a home for fishes?
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
Place your hand upon him; remember the battle and speak no more.
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
Behold, his hope will fail him, and in the sight of all, he will be thrown down.
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
I will not rouse him, as the cruel would do, for who is able to withstand my countenance?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
Who has given to me beforehand, so that I should repay him? All things that are under heaven are mine.
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
I will not spare him, nor his powerful words and counterfeit attempts at supplication.
13 Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
Who can reveal the beauty of his garment? And who can enter the middle of his mouth?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
Who can open the doors of his face? I gave fear to the circle of his teeth.
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
His body is like shields fused together, like dense scales pressed over one another.
16 Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
One is joined to another, and not even air can pass between them.
17 Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
They adhere to one another, and they hold themselves in place and will not be separated.
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
His sneezing has the brilliance of fire, and his eyes are like the eyelids of the morning.
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
Lamps proceed from his mouth, like torches of fire burning brightly.
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
Smoke passes out of his nostrils, like a pot that is heated and boiling.
21 Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
His breath causes coal to burn, and a flame comes forth from his mouth.
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
Strength dwells in his neck, and destitution goes before his presence.
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
The parts of his body work in harmony together. He will send lightning bolts against him, and they will not be carried to another place.
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
His heart will be as hard as a stone and as dense as a blacksmith’s anvil.
25 Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
When he will be raised up, the angels will be afraid, and, because they are terrified, they will purify themselves.
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
When a sword catches up with him, it will not be able to settle in, nor a spear, nor a breastplate.
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
For he will consider iron as if it were chaff, and brass as if it were rotten wood.
28 Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
The archer will not cause him to flee; the stones of the sling have been turned into stubble for him.
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
He will treat the hammer as if it were stubble, and he will ridicule those who brandish the spear.
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
The beams of the sun will be under him, and he will dispense gold to them as if it were clay.
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
He will make the depths of the sea boil like a pot, and he will set it to bubble just as ointments do.
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
A path will shine after him; he will esteem the abyss as if it were weakening with age.
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
There is no power on the earth that is being compared to him, who has been made so that he fears no one.
34 Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
He sees every prominent thing; he is king over all the sons of arrogance.

< Yobu 41 >