< Yobu 41 >
1 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
Canst thou draw out leviathan with a fishhook? Or press down his tongue with a cord?
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
Canst thou put a rope into his nose? Or pierce his jaw through with a hook?
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
Will he make many supplications unto thee? Or will he speak soft words unto thee?
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
Will he make a covenant with thee, That thou shouldest take him for a servant for ever?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
Wilt thou play with him as with a bird? Or wilt thou bind him for thy maidens?
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
Will the bands [of fishermen] make traffic of him? Will they part him among the merchants?
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
Canst thou fill his skin with barbed irons, Or his head with fish-spears?
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
Lay thy hand upon him; Remember the battle, and do so no more.
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
Behold, the hope of him is in vain: Will not one be cast down even at the sight of him?
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
None is so fierce that he dare stir him up; Who then is he that can stand before me?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
Who hath first given unto me, that I should repay him? [Whatsoever is] under the whole heaven is mine.
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
I will not keep silence concerning his limbs, Nor his mighty strength, nor his goodly frame.
13 Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
Who can strip off his outer garment? Who shall come within his jaws?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
Who can open the doors of his face? Round about his teeth is terror.
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
[His] strong scales are [his] pride, Shut up together [as with] a close seal.
16 Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
One is so near to another, That no air can come between them.
17 Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
They are joined one to another; They stick together, so that they cannot be sundered.
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
His sneezings flash forth light, And his eyes are like the eyelids of the morning.
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
Out of his mouth go burning torches, And sparks of fire leap forth.
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
Out of his nostrils a smoke goeth, As of a boiling pot and [burning] rushes.
21 Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
His breath kindleth coals, And a flame goeth forth from his mouth.
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
In his neck abideth strength, And terror danceth before him.
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
The flakes of his flesh are joined together: They are firm upon him; they cannot be moved.
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
His heart is as firm as a stone; Yea, firm as the nether millstone.
25 Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
When he raiseth himself up, the mighty are afraid: By reason of consternation they are beside themselves.
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
If one lay at him with the sword, it cannot avail; Nor the spear, the dart, nor the pointed shaft.
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
He counteth iron as straw, [And] brass as rotten wood.
28 Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
The arrow cannot make him flee: Sling-stones are turned with him into stubble.
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
Clubs are counted as stubble: He laugheth at the rushing of the javelin.
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
His underparts are [like] sharp potsherds: He spreadeth [as it were] a threshing-wain upon the mire.
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
He maketh the deep to boil like a pot: He maketh the sea like a pot of ointment.
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
He maketh a path to shine after him; One would think the deep to be hoary.
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
Upon earth there is not his like, That is made without fear.
34 Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
He beholdeth everything that is high: He is king over all the sons of pride.