< Yobu 41 >

1 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
Kan du trække Krokodillen op med Krog og binde dens Tunge med Snøre?
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
Kan du mon stikke et Siv i dens Snude, bore en Krog igennem dens Kæber?
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
Mon den vil trygle dig længe og give dig gode Ord?
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
Mon den vil indgå en Pagt med dig, så du får den til Træl for evigt?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
Han du mon lege med den som en Fugl og tøjre den for dine Pigebørn?
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
Falbyder Fiskerlauget den og stykker den ud mellem Sælgerne?
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
Mon du kan spække dens Hud med Kroge og med Harpuner dens Hoved?
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
Læg dog engang din Hånd på den! Du vil huske den Kamp og gør det ej mer.
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
Det Håb vilde blive til Skamme, alene ved Synet lå du der.
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
Ingen drister sig til at tirre den, hvem holder Stand imod den?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
Hvem møder den og slipper fra det hvem under hele Himlen?
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
Jeg tier ej om dens Lemmer, hvor stærk den er, hvor smukt den er skabt.
13 Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
Hvem har trukket dens Klædning af, trængt ind i dens dobbelte Panser?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
Hvem har åbnet dens Ansigts Døre? Rundt om dens Tænder er Rædsel.
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
Dens Ryg er Reder af Skjolde, dens Bryst er et Segl af Sten;
16 Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
de sidder tæt ved hverandre, Luft kommer ikke ind derimellem;
17 Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
de hænger fast ved hverandre, uadskilleligt griber de ind i hverandre.
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
Dens Nysen fremkalder strålende Lys, som Morgenrødens Øjenlåg er dens Øjne.
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
Ud af dens Gab farer Fakler, Ildgnister spruder der frem.
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
Em står ud af dens Næsebor som af en ophedet, kogende Kedel.
21 Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
Dens Ånde tænder som glødende Kul, Luer står ud af dens Gab.
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
Styrken bor på dens Hals, og Angsten hopper foran den.
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
Tæt sidder Kødets Knuder, som støbt til Kroppen; de rokkes ikke;
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
fast som Sten er dens Hjerte støbt, fast som den nederste Møllesten.
25 Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
Når den rejser sig, gyser Helte, fra Sans og Samling går de af Skræk.
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
Angriberens Sværd holder ikke Stand, ej Kastevåben, Spyd eller Pil.
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
Jern regner den kun for Halm og Kobber for trøsket Træ;
28 Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
Buens Søn slår den ikke på Flugt, Slyngens Sten bliver Strå for den,
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
Stridskøllen regnes for Rør, den ler ad det svirrende Spyd.
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
På Bugen er der skarpe Rande, dens Spor i Dyndet er som Tærskeslædens;
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
Dybet får den i Kog som en Gryde, en Salvekedel gør den af Floden;
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
bag den er der en lysende Sti, Dybet synes som Sølverhår.
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
Dens Lige findes ikke på Jord, den er skabt til ikke at frygte.
34 Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
Alt, hvad højt er, ræddes for den, den er Konge over alle stolte Dyr.

< Yobu 41 >