< Yobu 41 >

1 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
Vytáhneš-liž velryba udicí, aneb provazem pohříženým až k jazyku jeho?
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
Zdali dáš kroužek na chřípě jeho, aneb hákem probodneš čelist jeho?
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
Zdaž se obrátí k tobě s prosbami, aneb mluviti bude tobě lahodně?
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
Učiní-liž smlouvu s tebou? Přijmeš-liž jej za služebníka věčného?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
Zdaž budeš s ním hráti jako s ptáčkem, aneb přivážeš jej dětem svým?
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
Přistrojí-liž sobě hody z něho společníci, a rozdělí-liž jej mezi kupce?
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
Zdaž naplníš háky kůži jeho, a vidlicemi rybářskými hlavu jeho?
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
Vztáhni jen na něj ruku svou, a neučiníš zmínky o boji.
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
Aj, naděje o polapení jeho mylná jest. Zdaž i k spatření jeho člověk nebývá poražen?
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
Není žádného tak smělého, kdo by jej zbudil, kdož tedy postaví se přede mnou?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
Kdo mne čím předšel, abych se jemu odplacel? Cožkoli jest pode vším nebem, mé jest.
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
Nebudu mlčeti o údech jeho, a o síle výborného sformování jeho.
13 Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
Kdo odkryl svrchek oděvu jeho? S dvojitými udidly svými kdo k němu přistoupí?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
Vrata úst jeho kdo otevře? Okolo zubů jeho jest hrůza.
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
Šupiny jeho pevné jako štítové sevřené velmi tuze.
16 Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
Jedna druhé tak blízko jest, že ani vítr nevchází mezi ně.
17 Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
Jedna druhé se přídrží, a nedělí se.
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
Od kýchání jeho zažžehá se světlo, a oči jeho jsou jako záře svitání.
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
Z úst jeho jako pochodně vycházejí, a jiskry ohnivé vyskakují.
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
Z chřípí jeho vychází dým, jako z kotla vroucího aneb hrnce.
21 Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
Dýchání jeho uhlí rozpaluje, a plamen z úst jeho vychází.
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
V šíji jeho přebývá síla, a před ním utíká žalost.
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
Kusové masa jeho drží se spolu; celistvé jest v něm, aniž se rozdrobuje.
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
Srdce jeho tuhé jest jako kámen, tak tuhé, jako úlomek zpodního žernovu.
25 Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
Vyskýtání jeho bojí se nejsilnější, až se strachem i vyčišťují.
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
Meč stihající jej neostojí, ani kopí, šíp neb i pancíř.
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
Pokládá železo za plevy, ocel za dřevo shnilé.
28 Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
Nezahání ho střela, v stéblo obrací se jemu kamení prakové.
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
Za stéblo počítá střelbu, a posmívá se šermování kopím.
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
Pod ním ostré střepiny, stele sobě na věci špičaté jako na blátě.
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
Působí, aby vřelo v hlubině jako v kotle, a kormoutilo se moře jako v moždíři.
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
Za sebou patrnou činí stezku, až sezdá, že propast má šediny.
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
Žádného není na zemi jemu podobného, aby tak učiněn byl bez strachu.
34 Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
Cokoli vysokého jest, za nic pokládá, jest králem nade všemi šelmami.

< Yobu 41 >