< Yobu 41 >

1 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
你能用魚鉤釣上鱷魚嗎? 能用繩子壓下牠的舌頭嗎?
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
你能用繩索穿牠的鼻子嗎? 能用鉤穿牠的腮骨嗎?
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
牠豈向你連連懇求, 說柔和的話嗎?
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
豈肯與你立約, 使你拿牠永遠作奴僕嗎?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
你豈可拿牠當雀鳥玩耍嗎? 豈可為你的幼女將牠拴住嗎?
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
搭夥的漁夫豈可拿牠當貨物嗎? 能把牠分給商人嗎?
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
你能用倒鉤槍扎滿牠的皮, 能用魚叉叉滿牠的頭嗎?
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
你按手在牠身上,想與牠爭戰, 就不再這樣行吧!
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
人指望捉拿牠是徒然的; 一見牠,豈不喪膽嗎?
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
沒有那麼兇猛的人敢惹牠。 這樣,誰能在我面前站立得住呢?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
誰先給我甚麼,使我償還呢? 天下萬物都是我的。
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
論到鱷魚的肢體和其大力,並美好的骨骼, 我不能緘默不言。
13 Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
誰能剝牠的外衣? 誰能進牠上下牙骨之間呢?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
誰能開牠的腮頰? 牠牙齒四圍是可畏的。
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
牠以堅固的鱗甲為可誇, 緊緊合閉,封得嚴密。
16 Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
這鱗甲一一相連, 甚至氣不得透入其間,
17 Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
都是互相聯絡、膠結, 不能分離。
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
牠打噴嚏就發出光來; 牠眼睛好像早晨的光線。
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
從牠口中發出燒着的火把, 與飛迸的火星;
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
從牠鼻孔冒出煙來, 如燒開的鍋和點着的蘆葦。
21 Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
牠的氣點着煤炭, 有火焰從牠口中發出。
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
牠頸項中存着勁力; 在牠面前的都恐嚇蹦跳。
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
牠的肉塊互相聯絡, 緊貼其身,不能搖動。
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
牠的心結實如石頭, 如下磨石那樣結實。
25 Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
牠一起來,勇士都驚恐, 心裏慌亂,便都昏迷。
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
人若用刀,用槍,用標槍, 用尖槍扎牠,都是無用。
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
牠以鐵為乾草, 以銅為爛木。
28 Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
箭不能恐嚇牠使牠逃避; 彈石在牠看為碎稭。
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
棍棒算為禾稭; 牠嗤笑短槍颼的響聲。
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
牠肚腹下如尖瓦片; 牠如釘耙經過淤泥。
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
牠使深淵開滾如鍋, 使洋海如鍋中的膏油。
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
牠行的路隨後發光, 令人想深淵如同白髮。
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
在地上沒有像牠造的那樣, 無所懼怕。
34 Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
凡高大的,牠無不藐視; 牠在驕傲的水族上作王。

< Yobu 41 >