< Yobu 40 >
Además, Yahvé respondió a Job,
2 “Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
“¿Acaso el que discute puede contender con el Todopoderoso? El que discute con Dios, que responda”.
3 Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
Entonces Job respondió a Yahvé,
4 “Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
“He aquí que soy de poca monta. ¿Qué te voy a responder? Me pongo la mano en la boca.
5 Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
He hablado una vez y no voy a responder; Sí, dos veces, pero no seguiré adelante”.
6 Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
Entonces Yahvé respondió a Job desde el torbellino:
7 “Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
“Ahora prepárate como un hombre. Te interrogaré, y tú me responderás.
8 “Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
¿Acaso anularás mi juicio? ¿Me condenas para justificarte?
9 Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
¿O es que tienes un brazo como Dios? ¿Se puede tronar con una voz como la suya?
10 Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
“Ahora adórnate con excelencia y dignidad. Arréglate con honor y majestuosidad.
11 Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
Derrama la furia de tu ira. Mira a todos los que son orgullosos, y bájalos.
12 Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
Mira a todo el que es orgulloso, y humíllalo. Aplasta a los malvados en su lugar.
13 Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
Escóndelos juntos en el polvo. Ata sus rostros en el lugar oculto.
14 Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
Entonces también te admitiré que tu propia mano derecha puede salvarte.
15 “Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
“Mira ahora el behemoth, que yo he hecho igual que tú. Come hierba como un buey.
16 Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
Mira ahora, su fuerza está en sus muslos. Su fuerza está en los músculos de su vientre.
17 Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
Mueve su cola como un cedro. Los tendones de sus muslos están unidos.
18 Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
Sus huesos son como tubos de bronce. Sus miembros son como barras de hierro.
19 Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
Él es el principal de los caminos de Dios. El que lo hizo le da su espada.
20 Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
Ciertamente, las montañas producen alimento para él, donde juegan todos los animales del campo.
21 Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
Se acuesta bajo los árboles de loto, en la cobertura del carrizo, y el pantano.
22 Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
Los lotos lo cubren con su sombra. Los sauces del arroyo lo rodean.
23 Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
He aquí que si un río se desborda, no tiembla. Se muestra confiado, aunque el Jordán se hincha hasta la boca.
24 Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?
Lo tomará cualquiercuando esté de guardia, o atravesar su nariz con un lazo?