< Yobu 40 >

1 Yehova anati kwa Yobu:
Respondeu mais o Senhor a Job e disse:
2 “Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
Porventura o contender contra o Todo-poderoso é ensinar? quem quer reprehender a Deus, responda a estas coisas.
3 Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
Então Job respondeu ao Senhor, e disse:
4 “Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
Eis que sou vil; que te responderia eu? a minha mão ponho na minha bocca.
5 Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
Já uma vez tenho fallado, porém mais não responderei: ou ainda duas vezes, porém não proseguirei.
6 Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
Então o Senhor respondeu a Job desde a tempestade, e disse:
7 “Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
Ora, pois, cinge os teus lombos como varão; eu te perguntarei a ti, e tu ensina-me.
8 “Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
Porventura tambem farás tu vão o meu juizo? ou tu me condemnarás, para te justificares?
9 Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
Ou tens braço como Deus? ou podes trovejar com voz como a sua?
10 Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
Orna-te pois com excellencia e alteza; e veste-te de magestade e de gloria.
11 Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
Derrama os furores da tua ira, e attenta para todo o soberbo, e abate-o.
12 Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
Olha para todo o soberbo, e humilha-o, e atropella os impios no seu logar.
13 Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
Esconde-os juntamente no pó: ata-lhes os rostos em occulto.
14 Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
Então tambem eu a ti confessarei que a tua mão direita te haverá livrado.
15 “Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
Vês aqui a Behemoth, que eu fiz comtigo, que come a herva como o boi.
16 Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
Eis que a sua força está nos seus lombos, e o seu poder no umbigo do seu ventre.
17 Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
Quando quer, move a sua cauda como cedro: os nervos das suas coxas estão entretecidos.
18 Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
Os seus ossos são como coxas de bronze: a sua ossada é como barras de ferro.
19 Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
Elle é obra prima dos caminhos de Deus: o que o fez lhe apegou a sua espada.
20 Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
Em verdade os montes lhe produzem pasto, onde todos os animaes do campo folgam.
21 Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
Deita-se debaixo das arvores sombrias, no esconderijo das canas e da lama.
22 Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
As arvores sombrias o cobrem, com sua sombra: os salgueiros do ribeiro o cercam.
23 Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
Eis que um rio trasborda, e elle não se apressa, confiando que o Jordão possa entrar na sua bocca.
24 Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?
Podel-o-hiam porventura caçar á vista de seus olhos? ou com laços lhe furar os narizes?

< Yobu 40 >