< Yobu 40 >

1 Yehova anati kwa Yobu:
Et adiecit Dominus, et locutus est ad Iob:
2 “Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
Numquid qui contendit cum Deo, tam facile conquiescit? utique qui arguit Deum, debet respondere ei.
3 Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
Respondens autem Iob Domino, dixit:
4 “Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
Qui leviter locutus sum, respondere quid possum? manum meam ponam super os meum.
5 Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
Unum locutus sum, quod utinam non dixissem: et alterum, quibus ultra non addam.
6 Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
Respondens autem Dominus Iob de turbine, dixit:
7 “Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
Accinge sicut vir lumbos tuos: interrogabo te: et indica mihi.
8 “Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
Numquid irritum facies iudicium meum: et condemnabis me, ut tu iustificeris?
9 Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
Et si habes brachium sicut Deus, et si voce simili tonas?
10 Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
Circumda tibi decorem, et in sublime erigere, et esto gloriosus, et speciosis induere vestibus.
11 Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
Disperge superbos in furore tuo, et respiciens omnem arrogantem humilia.
12 Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
Respice cunctos superbos, et confunde eos, et contere impios in loco suo.
13 Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
Absconde eos in pulvere simul, et facies eorum demerge in foveam:
14 Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
Et ego confitebor quod salvare te possit dextera tua.
15 “Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
Ecce, Behemoth, quem feci tecum, foenum quasi bos comedet:
16 Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
Fortitudo eius in lumbis eius, et virtus illius in umbilico ventris eius.
17 Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
Stringit caudam suam quasi cedrum, nervi testiculorum eius perplexi sunt.
18 Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
Ossa eius velut fistulae aeris, cartilago illius quasi laminae ferreae.
19 Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
Ipse est principium viarum Dei, qui fecit eum, applicabit gladium eius.
20 Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
Huic montes herbas ferunt: omnes bestiae agri ludent ibi.
21 Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
Sub umbra dormit in secreto calami, et in locis humentibus.
22 Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
Protegunt umbrae umbram eius, circumdabunt eum salices torrentis.
23 Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
Ecce, absorbebit fluvium, et non mirabitur: et habet fiduciam quod influat Iordanis in os eius.
24 Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?
In oculis eius quasi hamo capiet eum, et in sudibus perforabit nares eius.

< Yobu 40 >