< Yobu 40 >
L'Eternel prit encore la parole, et dit:
2 “Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
Celui qui conteste avec le Tout-puissant, lui apprendra-t-il quelque chose? Que celui qui dispute avec Dieu, réponde à ceci.
3 Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
Alors Job répondit à l'Eternel, et dit:
4 “Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
Voici, je suis un homme vil; que te répondrais-je? Je mettrai ma main sur ma bouche.
5 Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
J'ai parlé une fois, mais je ne répondrai plus; j'ai même parlé deux fois, mais je n'y retournerai plus.
6 Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
Et l'Eternel parla encore à Job du milieu d'un tourbillon, et lui dit:
7 “Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
Ceins maintenant tes reins comme un vaillant homme; je t'interrogerai, et tu m'enseigneras.
8 “Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
Anéantiras-tu mon jugement? me condamneras-tu pour te justifier?
9 Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
Et as-tu un bras comme le [Dieu] Fort? tonnes-tu de la voix comme lui?
10 Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
Pare-toi maintenant de magnificence et de grandeur, et revêts-toi de majesté et de gloire.
11 Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
Répands les ardeurs de ta colère, regarde tout orgueilleux, et l'abats.
12 Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
Regarde tout orgueilleux, abaisse-le, et froisse les méchants sur la place.
13 Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
Cache-les tous ensemble dans la poudre, et bande leur visage dans un lieu caché.
14 Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
Alors je te donnerai moi-même cette louange, que ta droite t'aura sauvé.
15 “Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
Or voilà le Béhémoth que j'ai fait avec toi; il mange le foin comme le bœuf.
16 Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
Voilà maintenant, sa force est en ses flancs, et sa vertu est dans le nombril de son ventre.
17 Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
Il remue sa queue, qui est comme un cèdre; les nerfs de ses épouvantements sont entrelacés.
18 Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
Ses os sont des barres d'airain, [et] ses menus os sont comme des barreaux de fer.
19 Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
C'est le chef-d'œuvre du [Dieu] Fort; celui qui l'a fait lui a donné son épée.
20 Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
Et les montagnes lui rapportent leur revenu, et c'est là que se jouent toutes les bêtes des champs.
21 Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
Il se couche dans les lieux où il y a de l'ombre, au milieu des roseaux et des marécages.
22 Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
Les arbres touffus le couvrent de leur ombre, et les saules des torrents l'environnent.
23 Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
Voilà, il engloutit une rivière [en buvant], et il ne s'en retire pas vite; et il ne s'étonnerait pas quand le Jourdain se dégorgerait dans sa gueule.
24 Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?
Il l'engloutit en le voyant, et son nez passe au travers des empêchements qu'il rencontre.