< Yobu 40 >

1 Yehova anati kwa Yobu:
Then Yahweh said to Job,
2 “Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
“Do you still want to argue with me, the Almighty One? Since you criticize me, (you should be able to answer my questions!/why are you not able to answer my questions?) [RHQ]”
3 Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
Then Job replied to Yahweh,
4 “Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
“[Now I realize that] I am completely worthless. So (how could I answer [those questions]?/I could not possibly answer [those questions]!) [RHQ] I will put my hand over my mouth [and not say anything].
5 Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
I have already said more than I should have said, so now I will say nothing more.”
6 Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
Then Yahweh [again] spoke to Job from inside the great windstorm. He said,
7 “Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
“I want to ask you some [more] questions. So as men prepare themselves for a difficult task [MET], prepare yourself again to answer some [more] questions.
8 “Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
“Are you going to accuse me and say that I am unjust? Are you going to say that what I have done is wrong, in order that you can say that what you have done is right?
9 Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
Are you as powerful [MTY] as I am? Can your voice sound [as loud] as thunder, as mine can?
10 Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
[If you can do that], put on the robes that show that you are glorious and are greatly honored!
11 Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
Show that you are very angry; show that you have the right/authority to humble people who are [very] proud!
12 Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
Humble those proud people [just] by looking at them [angrily] Crush wicked people quickly!
13 Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
Bury them in the ground! Send them to the place where dead people are, where they will not be able to get out!
14 Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
After you do that, I will congratulate/praise you and say that [truly] you can save yourself by your own ability/power.
15 “Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
“Think [also] about the huge animals that live near the water. I made you, and I made them also. They eat grass, like oxen do.
16 Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
Their legs/thighs are [very] strong, and the muscles of their bellies are [very] powerful.
17 Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
Their tails are stiff (OR, bend down) like the branches of a cedar tree. The sinews/muscles of their thighs are close together.
18 Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
Their [thigh] bones are [like] tubes [made] of bronze, and the bones of their legs are like bars [made] of iron.
19 Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
They are among the strongest of the animals that I made, and I, who created them, am the only one who can kill them.
20 Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
On the hills grows food [PRS] for them to eat while many [HYP] other wild animals play nearby.
21 Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
They lie down [in the water] under the lotus plants; they hide in [tall] reeds in the swamps.
22 Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
Those huge animals find shade under the lotus plants, and they are surrounded by poplar trees.
23 Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
They are not disturbed by raging/swiftly-flowing rivers; they are not even disturbed/frightened when [rivers like the] Jordan [River] rush over them.
24 Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?
No one can [RHQ] catch them by blinding their eyes or by piercing their noses with [the teeth of] a trap!”

< Yobu 40 >