< Yobu 40 >
Nu vervolgde Jahweh tot Job, en sprak:
2 “Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
Zal nu de bediller van den Almachtige zwijgen; Of weet de vitter op God hier nog antwoord op?
3 Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
Maar Job antwoordde Jahweh, en sprak:
4 “Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
Ik ben lichtzinnig geweest: Wat zou ik hierop kunnen zeggen; Ik leg mijn hand op mijn mond.
5 Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
Ik heb eens gesproken, maar doe het niet weer; Tweemaal, maar ik begin niet opnieuw!
6 Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
Maar Jahweh vervolgde, en sprak tot Job in de storm
7 “Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
Omgord uw lenden als een man, Ik zal u vragen stellen, gij moogt Mij leren!
8 “Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
Wilt ge ook nu nog mijn gerechtigheid loochenen, Mij in het ongelijk stellen, om gelijk te hebben?
9 Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
Hebt ge dan een arm, zoals God, Kunt ge donderen met een stem als de zijne?
10 Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
Tooi u dan eens met grootheid en luister, Bekleed u met glorie en majesteit!
11 Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
Stort eens uw toorn in stromen uit, En verneder, wat trots is, met uw blik;
12 Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
Zie op alle hoogmoedigen neer, en trap ze ineen, Verpletter de bozen terstond;
13 Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
Stop ze allen weg in de grond, Zet ze gevangen in het verborgen oord:
14 Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
Dan zal Ik de eerste zijn, die u prijst, Omdat het uw rechterhand is, die u helpt!
15 “Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
Maar zie, daar staat het Nijlpaard, dat Ik heb geschapen, Het vreet gras als een rund.
16 Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
Zie eens, wat kracht in zijn lenden, Wat sterkte in de spieren van zijn buik!
17 Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
Hij spant zijn staart als een ceder, De spieren van zijn dijen tot een bundel;
18 Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
Zijn schonken zijn koperen buizen, Zijn knoken als ijzeren staven.
19 Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
Hij is het meesterwerk van God Gemaakt, om over zijn buurtschap te heersen!
20 Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
Ja, de bergen brengen hem schatting, Met al het wild, dat daar speelt;
21 Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
Onder de lotus vleit hij zich neer, Verscholen in riet en moeras;
22 Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
Lotusstruiken beschutten hem met hun schaduw, De waterwilgen staan om hem heen;
23 Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
Al raast de stroom, hij is niet bang, Onverschrokken, al stijgt de Jordaan tot zijn muil.
24 Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?
Wie durft hem bij zijn ogen grijpen, Zijn neus met harpoenen doorboren!