< Yobu 4 >
1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Y RESPONDIÓ Eliphaz el Temanita, y dijo:
2 “Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
Si probáremos á hablarte, serte ha molesto; mas ¿quién podrá detener las palabras?
3 Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
He aquí, tú enseñabas á muchos, y las manos flacas corroborabas;
4 Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
Al que vacilaba, enderezaban tus palabras, y esforzabas las rodillas que decaían.
5 Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
Mas ahora que [el mal] sobre ti ha venido, te es duro; y cuando ha llegado hasta ti, te turbas.
6 Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
¿Es este tu temor, tu confianza, tu esperanza, y la perfección de tus caminos?
7 “Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
Recapacita ahora, ¿quién que fuera inocente se perdiera? y ¿en dónde los rectos fueron cortados?
8 Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
Como yo he visto, los que aran iniquidad y siembran injuria, la siegan.
9 Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
Perecen por el aliento de Dios, y por el espíritu de su furor son consumidos.
10 Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
El bramido del león, y la voz del león, y los dientes de los leoncillos son quebrantados.
11 Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
El león viejo perece por falta de presa, y los hijos del león son esparcidos.
12 “Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
El negocio también me era á mí oculto; mas mi oído ha percibido algo de ello.
13 Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
En imaginaciones de visiones nocturnas, cuando el sueño cae sobre los hombres,
14 ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
Sobrevínome un espanto y un temblor, que estremeció todos mis huesos:
15 Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
Y un espíritu pasó por delante de mí, que hizo se erizara el pelo de mi carne.
16 Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
Paróse un fantasma delante de mis ojos, cuyo rostro yo no conocí, y quedo, oí que decía:
17 ‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
¿Si será el hombre más justo que Dios? ¿si será el varón más limpio que el que lo hizo?
18 Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
He aquí que en sus siervos no confía, y notó necedad en sus ángeles;
19 nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
¡Cuánto más en los que habitan en casas de lodo, cuyo fundamento está en el polvo, y que serán quebrantados de la polilla!
20 Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
De la mañana á la tarde son quebrantados, y se pierden para siempre, sin haber quien lo considere.
21 Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’
¿Su hermosura, no se pierde con ellos mismos? Mueren, y sin sabiduría.