< Yobu 4 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Então Elifaz, o Temanita, respondeu,
2 “Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
“Se alguém se aventurar a falar com você, você ficará de luto? Mas quem pode se impedir de falar?
3 Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
Veja, você já instruiu muitos, você fortaleceu as mãos fracas.
4 Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
Suas palavras apoiaram aquele que estava caindo, você tornou os joelhos frágeis e firmes.
5 Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
Mas agora chegou até você, e você desmaia. Isso o toca, e você está perturbado.
6 Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
Sua piedade não é sua confiança? A integridade de seus caminhos não é sua esperança?
7 “Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
“Lembre-se, agora, quem pereceu, sendo inocente? Ou onde foram os cortes verticais?
8 Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
According ao que tenho visto, aqueles que lavram a iniqüidade e semear problemas, colher o mesmo.
9 Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
Pelo sopro de Deus eles perecem. Pela explosão de sua raiva eles são consumidos.
10 Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
O rugido do leão, e a voz do leão feroz, os dentes dos leões jovens, estão quebrados.
11 Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
O velho leão perece por falta de presa. As crias da leoa estão dispersas no exterior.
12 “Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
“Agora uma coisa foi trazida secretamente para mim. Meu ouvido recebeu um sussurro disso.
13 Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
Em pensamentos das visões da noite, quando o sono profundo cai sobre os homens,
14 ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
o medo veio sobre mim, e tremendo, o que fez todos os meus ossos tremerem.
15 Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
Então um espírito passou diante do meu rosto. Os cabelos da minha carne se levantaram.
16 Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
Ficou parado, mas eu não conseguia discernir sua aparência. Um formulário estava diante dos meus olhos. Silêncio, então eu ouvi uma voz, dizendo,
17 ‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
'O homem mortal deve ser mais justo que Deus? Será que um homem deve ser mais puro que seu Criador?
18 Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
Eis que ele não deposita confiança em seus servos. Ele acusa seus anjos de erro.
19 nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
Quanto mais aqueles que moram em casas de barro, cuja base está no pó, que são esmagados diante da traça!
20 Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
Between de manhã e à noite eles são destruídos. Eles perecem para sempre sem nada a ver com isso.
21 Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’
O cordão da barraca deles não está arrancado dentro deles? Eles morrem, e isso sem sabedoria”.

< Yobu 4 >