< Yobu 4 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Wtedy Elifaz z Temanu odpowiedział:
2 “Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
Jeśli będziemy rozmawiać z tobą, nie będzie ci przykro? Ale któż może się od mówienia powstrzymać?
3 Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
Oto nauczałeś wielu i ręce słabe umocniłeś.
4 Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
Twoje słowa podnosiły upadającego, a omdlałe kolana wzmacniałeś.
5 Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
A teraz, gdy [to] przyszło na ciebie, opadasz z sił, dotknęło cię i się trwożysz.
6 Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
Czy twoja bojaźń nie była twoją ufnością, a prawość twoich dróg – twoją nadzieją?
7 “Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
Przypomnij sobie, proszę, czy kiedykolwiek zginął ktoś niewinny? Albo gdzie sprawiedliwych wytępiono?
8 Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
Według tego, co zauważyłem, ci, którzy orzą zło i sieją niegodziwość, zbierają je.
9 Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
Od tchnienia Boga giną i od powiewu jego gniewu niszczeją.
10 Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
Ryk lwa, głos dzikiego lwa i zęby lwiątek są złamane.
11 Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
Lew ginie z braku łupu i młode lwicy rozpraszają się.
12 “Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
Oto potajemnie doszło do mnie słowo i moje ucho usłyszało szept.
13 Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
W rozmyślaniu o nocnych widzeniach, gdy twardy sen spada na ludzi;
14 ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
Ogarnęły mnie strach i drżenie, od których wszystkie moje kości zadrżały.
15 Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
Wtedy duch przeszedł przed moją twarzą, zjeżyły się włosy na moim ciele.
16 Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
Stanął, lecz nie rozpoznałem jego wyglądu, [tylko jakiś] kształt [był] przed moimi oczami; nastała cisza, a potem usłyszałem głos [mówiący]:
17 ‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
Czy śmiertelny człowiek może być sprawiedliwszy niż Bóg? Czy człowiek [może być] czystszy niż jego Stwórca?
18 Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
Oto swoim sługom nie ufa i w swoich aniołach dostrzega braki;
19 nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
O ileż bardziej w tych, którzy mieszkają w domach glinianych, których podstawa jest w prochu – łatwiej [ich] zgnieść niż mola.
20 Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
Od poranka aż do wieczora są gładzeni; giną na wieki, a nikt [tego] nie zauważa.
21 Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’
Czy ich wspaniałość nie przemija wraz z nimi? Umierają, ale nie w mądrości.

< Yobu 4 >