< Yobu 4 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
UElifazi umThemani wasephendula wathi:
2 “Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
Uba sizama ilizwi kuwe, uzadabuka yini? Kodwa ngubani ongazibamba emazwini?
3 Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
Khangela, uqondisile abanengi, waqinisa izandla ezibuthakathaka.
4 Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
Amazwi akho amvusile okhubekayo, waqinisa amadolo axegayo.
5 Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
Kodwa khathesi kufikile kuwe, uyadinwa; kuyakuthinta wena, utshaywa luvalo.
6 Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
Ukwesaba kwakho uNkulunkulu kakusiso isibindi sakho yini, lobuqotho bendlela zakho ithemba lakho?
7 “Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
Akukhumbule, ngubani owake wachithwa engelacala? Kumbe abalungileyo bake baqunywa ngaphi?
8 Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
Njengengikubonileyo, abalima ububi behlanyela udubo, bavuna khona.
9 Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
Ngokuphephetha kukaNkulunkulu bayabhubha, langokuphefumula kwamakhala akhe bayaphela.
10 Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
Ukubhonga kwesilwane, lelizwi lesilwane esesabekayo, lamazinyo amabhongo esilwane, kwephukile.
11 Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
Isilwane esidala siyabhubha ngokuswela impango, lemidlwane yesilwanekazi isabalale.
12 “Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
Ngasenginyenyezelwa ilizwi, lendlebe yami yemukela okuncinyane kwalo.
13 Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
Phakathi kwemicabango yemibono yebusuku, lapho ubuthongo obukhulu busehlela abantu,
14 ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
ukwesaba kwangifikela lokuthuthumela okwenza ubunengi bamathambo ami baqhaqhazela.
15 Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
Kwasekusedlula umoya ebusweni bami, loboya benyama yami bavuka.
16 Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
Wema, kodwa angikuqondanga ukubonakala kwawo; isimo sasiphambi kwamehlo ami; kwathula, ngasengisizwa ilizwi lisithi:
17 ‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
Kambe umuntu angalunga okwedlula uNkulunkulu? Umuntu angahlambuluka okwedlula uMenzi wakhe yini?
18 Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
Khangela, kazithembi inceku zakhe, lengilosi zakhe uthi zingabaphosisi.
19 nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
Kangakanani abahlala endlini zebumba, abasisekelo sabo sisethulini, abachotshozwa phambi kwenundu.
20 Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
Bakhandwa kusukela ekuseni kuze kube kusihlwa, kungelakunanzwa bayabhubha kuze kube nininini.
21 Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’
Ubuhle babo kabususwa labo yini? Bayafa kodwa bengalanhlakanipho.

< Yobu 4 >