< Yobu 4 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Respondens autem Eliphaz Themanites, dixit:
2 “Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
Si coeperimus loqui tibi, forsitan moleste accipies, sed conceptum sermonem tenere quis poterit?
3 Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
Ecce docuisti multos, et manus lassas roborasti:
4 Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
Vacillantes confirmaverunt sermones tui, et genua trementia confortasti:
5 Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
Nunc autem venit super te plaga, et defecisti: tetigit te, et conturbatus es.
6 Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
Ubi est timor tuus, fortitudo tua, patientia tua, et perfectio viarum tuarum?
7 “Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
Recordare obsecro te, quis umquam innocens periit? aut quando recti deleti sunt?
8 Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
Quin potius vidi eos, qui operantur iniquitatem, et seminant dolores, et metunt eos,
9 Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
Flante Deo perisse, et spiritu irae eius esse consumptos:
10 Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
Rugitus leonis, et vox leaenae, et dentes catulorum leonum contriti sunt.
11 Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
Tigris periit, eo quod non haberet praedam, et catuli leonis dissipati sunt.
12 “Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
Porro ad me dictum est verbum absconditum, et quasi furtive suscepit auris mea venas susurri eius.
13 Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
In horrore visionis nocturnae, quando solet sopor occupare homines,
14 ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
Pavor tenuit me, et tremor, et omnia ossa mea perterrita sunt:
15 Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
Et cum spiritus me praesente transiret, inhorruerunt pili carnis meae.
16 Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
Stetit quidam, cuius non agnoscebam vultum, imago coram oculis meis, et vocem quasi aurae lenis audivi.
17 ‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
Numquid homo, Dei comparatione iustificabitur, aut factore suo purior erit vir?
18 Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
Ecce qui serviunt ei, non sunt stabiles, et in angelis suis reperit pravitatem:
19 nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
Quanto magis hi qui habitant domos luteas, qui terrenum habent fundamentum, consumentur velut a tinea?
20 Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
De mane usque ad vesperam succidentur: et quia nullus intelligit, in aeternum peribunt.
21 Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’
Qui autem reliqui fuerint, auferentur ex eis: morientur, et non in sapientia.

< Yobu 4 >