< Yobu 4 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
ויען אליפז התימני ויאמר
2 “Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
הנסה דבר אליך תלאה ועצר במלין מי יוכל
3 Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
הנה יסרת רבים וידים רפות תחזק
4 Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
כושל יקימון מליך וברכים כרעות תאמץ
5 Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
כי עתה תבוא אליך ותלא תגע עדיך ותבהל
6 Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
הלא יראתך כסלתך תקותך ותם דרכיך
7 “Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
זכר-נא--מי הוא נקי אבד ואיפה ישרים נכחדו
8 Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
כאשר ראיתי חרשי און וזרעי עמל יקצרהו
9 Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
מנשמת אלוה יאבדו ומרוח אפו יכלו
10 Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
שאגת אריה וקול שחל ושני כפירים נתעו
11 Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
ליש אבד מבלי-טרף ובני לביא יתפרדו
12 “Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
ואלי דבר יגנב ותקח אזני שמץ מנהו
13 Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
בשעפים מחזינות לילה בנפל תרדמה על-אנשים
14 ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
פחד קראני ורעדה ורב עצמותי הפחיד
15 Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
ורוח על-פני יחלף תסמר שערת בשרי
16 Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
יעמד ולא אכיר מראהו-- תמונה לנגד עיני דממה וקול אשמע
17 ‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
האנוש מאלוה יצדק אם מעשהו יטהר-גבר
18 Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
הן בעבדיו לא יאמין ובמלאכיו ישים תהלה
19 nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
אף שכני בתי-חמר--אשר-בעפר יסודם ידכאום לפני-עש
20 Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
מבקר לערב יכתו מבלי משים לנצח יאבדו
21 Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’
הלא-נסע יתרם בם ימותו ולא בחכמה

< Yobu 4 >