< Yobu 4 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Et Eliphaz de Théman répondit et dit:
2 “Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
Tenter de te parler, sera-ce t'être importun? Mais qui pourrait s'empêcher de parler?
3 Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
Voici, tu redressas beaucoup d'hommes, et fortifias des mains débiles,
4 Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
ta parole releva ceux qui bronchaient, et tu raffermis les genoux qui pliaient.
5 Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
Maintenant que ton tour vient, tu faiblis! maintenant que tu es atteint, tu es éperdu!
6 Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
En ta crainte de Dieu ne te confies-tu pas, et ton espoir n'est-il pas l'innocence de ta vie?
7 “Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
Eh! penses-y! quel innocent a péri, et où les justes ont-ils été détruits?
8 Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
Ainsi que je l'ai vu, ceux qui cultivent le mal, et sèment la malice, l'ont pour récolte;
9 Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
au souffle de Dieu ils périssent, et le vent de son courroux les consume;
10 Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
le cri du lion, et la voix du rugissant, et les dents des lionceaux leur sont ôtés,
11 Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
le vieux lion périt faute de proie, et les petits de la lionne sont dispersés.
12 “Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
Mais une parole me fut dite à la dérobée, et mon oreille en a saisi le murmure.
13 Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
Les visions de la nuit agitaient mes pensées, à l'heure où le sommeil accable les humains:
14 ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
une terreur me saisit avec un tremblement, et le frisson parcourut tous mes os;
15 Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
et un esprit passa devant mon visage, et sur mon corps mes cheveux se dressèrent;
16 Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
une figure dont l'air m'est inconnu, s'arrêta en face de mes yeux; il y eut un frémissement, et j'entendis une voix:
17 ‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
« L'homme est-il juste devant Dieu, et le mortel, pur devant son créateur?
18 Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
Voici, de ses serviteurs Il se défie, et dans ses anges mêmes Il trouve du péché;
19 nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
que sera-ce donc des habitants de maisons d'argile, dont les fondements posent sur la poudre? Ils sont détruits comme par la teigne,
20 Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
d'un matin à un soir ils sont mis en pièces; sans qu'on y prenne garde, ils périssent pour toujours;
21 Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’
leur magnificence ne leur est-elle pas ôtée? Ils meurent, et n'ont pas la sagesse. »

< Yobu 4 >