< Yobu 4 >
1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Alors Éliphaz, le Thémanite, prit la parole,
2 “Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
« Si quelqu'un s'aventure à parler avec toi, seras-tu affligé? Mais qui peut se retenir de parler?
3 Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
Voici, vous avez instruit beaucoup de gens, vous avez renforcé les mains faibles.
4 Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
Tes paroles ont soutenu celui qui tombait, tu as raffermi les genoux faibles.
5 Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
Mais maintenant, cela t'est arrivé, et tu t'es évanoui. Il vous touche, et vous êtes troublé.
6 Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
Votre piété n'est-elle pas votre confiance? L'intégrité de vos voies n'est-elle pas votre espoir?
7 “Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
« Souviens-toi maintenant de celui qui a péri, étant innocent? Ou bien où ont été coupés les montants?
8 Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
Selon ce que j'ai vu, ceux qui labourent l'iniquité qui sèment le trouble, récoltent la même chose.
9 Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
Par le souffle de Dieu, ils périssent. Ils sont consumés par le souffle de sa colère.
10 Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
Le rugissement du lion, et la voix du lion féroce, les dents des jeunes lions, sont cassées.
11 Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
Le vieux lion périt par manque de proie. Les petits de la lionne sont dispersés.
12 “Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
« Or, une chose m'a été rapportée en secret. Mon oreille en a reçu un murmure.
13 Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
Dans les pensées des visions de la nuit, quand le sommeil profond tombe sur les hommes,
14 ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
La peur m'a saisi, et le tremblement, qui a fait trembler tous mes os.
15 Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
Alors un esprit passa devant ma face. Les poils de ma chair se sont dressés.
16 Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
Elle était immobile, mais je ne pouvais pas discerner son apparence. Une forme était devant mes yeux. Silence, puis j'ai entendu une voix, disant,
17 ‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
« Un homme mortel serait-il plus juste que Dieu? Un homme peut-il être plus pur que son créateur?
18 Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
Voici, il ne fait pas confiance à ses serviteurs. Il charge ses anges d'erreurs.
19 nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
Combien plus ceux qui habitent des maisons d'argile, dont les fondations sont dans la poussière, qui sont écrasés par la mite!
20 Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
Entre le matin et le soir, ils sont détruits. Ils périssent à jamais sans que personne ne s'en aperçoive.
21 Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’
Leur corde de tente n'est-elle pas arrachée en eux? Ils meurent, et cela sans sagesse.