< Yobu 4 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Forsothe Eliphat Themanytes answeride, and seide,
2 “Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
If we bigynnen to speke to thee, in hap thou schalt take it heuyli; but who may holde a word conseyued?
3 Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
Lo! thou hast tauyt ful many men, and thou hast strengthid hondis maad feynt.
4 Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
Thi wordis confermyden men doutynge, and thou coumfortidist knees tremblynge.
5 Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
But now a wounde is comun on thee, and thou hast failid; it touchide thee, and thou art disturblid.
6 Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
Where is thi drede, thi strengthe, and thi pacience, and the perfeccioun of thi weies?
7 “Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
Y biseche thee, haue thou mynde, what innocent man perischide euere, ethir whanne riytful men weren doon awei?
8 Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
Certis rathir Y siy hem, that worchen wickidnesse, and sowen sorewis,
9 Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
and repen tho, to haue perischid bi God blowynge, and to be wastid bi the spirit of his ire.
10 Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
The roryng of a lioun, and the vois of a lionesse, and the teeth of `whelpis of liouns ben al to-brokun.
11 Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
Tigris perischide, for sche hadde not prey; and the whelpis of a lioun ben distried.
12 “Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
Certis an hid word was seid to me, and myn eere took as theueli the veynes of priuy noise therof.
13 Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
In the hidousnesse of `nyytis siyt, whanne heuy sleep is wont to occupie men,
14 ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
drede and tremblyng helde me; and alle my boonys weren aferd.
15 Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
And whanne the spirit `yede in my presence, the heiris of `my fleisch hadden hidousnesse.
16 Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
Oon stood, whos chere Y knewe not, an ymage bifor myn iyen; and Y herde a vois as of softe wynd.
17 ‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
Whether a man schal be maad iust in comparisoun of God? ethir whethir a man schal be clennere than his Makere?
18 Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
Lo! thei that seruen hym ben not stidefast; and he findith schrewidnesse in hise aungels.
19 nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
Hou myche more thei that dwellen in housis of cley, that han an ertheli foundement, schulen be wastyd as of a mouyte.
20 Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
Fro morewtid til to euentid thei schulen be kit doun; and for no man vndurstondith, thei schulen perische with outen ende.
21 Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’
Sotheli thei, that ben residue, schulen be takun awei; thei schulen die, and not in wisdom.

< Yobu 4 >