< Yobu 4 >
1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Så tog Temaniten Elifaz til Orde og sagde:
2 “Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
Ærgrer det dig, om man taler til dig? Men hvem kan her være tavs?
3 Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
Du har selv talt mange til Rette og styrket de slappe Hænder,
4 Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
dine Ord holdt den segnende oppe, vaklende Knæ gav du Kraft.
5 Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
Men nu det gælder dig selv, så taber du Modet, nu det rammer dig selv, er du slaget af Skræk!
6 Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
Er ikke din Gudsfrygt din Tillid, din fromme Færd dit Håb?
7 “Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
Tænk efter! Hvem gik uskyldig til Grunde, hvor gik retsindige under?
8 Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
Men det har jeg set: Hvo Uret pløjer og sår Fortræd, de høster det selv.
9 Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
For Guds Ånd går de til Grunde, for hans Vredes Pust går de til.
10 Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
Løvens Brøl og Vilddyrets Glam Ungløvernes Tænder slås ud;
11 Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
Løven omkommer af Mangel på Rov, og Løveungerne spredes.
12 “Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
Der sneg sig til mig et Ord mit Øre opfanged dets Hvisken
13 Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
i Nattesynernes Tanker, da Dvale sank over Mennesker;
14 ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
Angst og Skælven kom over mig, alle mine Ledemod skjalv;
15 Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
et Pust strøg over mit Ansigt, Hårene rejste sig på min Krop.
16 Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
Så stod det stille! Jeg sansed ikke, hvordan det så ud; en Skikkelse stod for mit Øje, jeg hørte en hviskende Stemme:
17 ‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
"Har et Menneske Ret for Gud, mon en Mand er ren for sin Skaber?
18 Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
End ikke sine Tjenere tror han, hos sine Engle finder han Fejl,
19 nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
endsige hos dem, der bor i en Hytte af Ler og har deres Grundvold i Støvet!
20 Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
De knuses ligesom Møl, imellem Morgen og Aften, de sønderslås uden at ænses, for evigt går de til Grunde.
21 Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’
Rives ej deres Teltreb ud? De dør, men ikke i Visdom."