< Yobu 4 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Jemuž odpovídaje Elifaz Temanský, řekl:
2 “Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
Počneme-li mluviti s tebou, neponeseš-liž toho těžce? Ale kdož by se zdržeti mohl, aby neměl mluviti?
3 Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
Aj, učívals mnohé, a rukou opuštěných jsi posiloval.
4 Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
Padajícího pozdvihovals řečmi svými, a kolena zemdlená jsi zmocňoval.
5 Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
Nyní pak, jakž toto přišlo na tebe, těžce to neseš, a jakž tě dotklo, předěšen jsi.
6 Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
Nebylo-liž náboženství tvé nadějí tvou, a upřímost cest tvých očekáváním tvým?
7 “Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
Rozpomeň se, prosím, kdo jest kdy nevinný zahynul? Aneb kde upřímí vyhlazeni jsou?
8 Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
Jakož jsem já vídal ty, kteříž orali nepravost, a rozsívali převrácenost, že ji i žali.
9 Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
Od dchnutí Božího hynou, a duchem prchlivosti jeho v nic obracíni bývají.
10 Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
Řvání lva a hlas lvice a zubové mladých lvíčat setříni bývají.
11 Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
Hyne lev, že nemá loupeže, a lvíčata mladá rozptýlena bývají.
12 “Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
Nebo i tajně doneslo se mne slovo, a pochopilo ucho mé něco maličko toho.
13 Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
V přemyšlováních z vidění nočních, když připadá tvrdý sen na lidi,
14 ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
Strach připadl na mne a lekání, kteréž předěsilo všecky kosti mé.
15 Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
Duch zajisté před tváří mou šel, tak že vlasové vstávali na těle mém.
16 Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
Zastavil se, ale neznal jsem tváři jeho; tvárnost jen byla před očima mýma. Mezi tím mlče, slyšel jsem hlas:
17 ‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
Zdaliž může člověk spravedlivějším býti než Bůh, aneb muž čistším nad toho, kterýž ho učinil?
18 Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
Ano mezi služebníky jeho není dokonalosti, a při andělích svých zanechal nedostatku.
19 nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
Èím více při těch, kteříž bydlejí v domích hliněných, jejichž základ jest na prachu, a setříni bývají snáze než mol.
20 Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
Od jitra až do večera stíráni bývají, a kdož toho nerozvažují, na věky zahynou.
21 Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’
Zdaliž nepomíjí sláva jejich s nimi? Umírají, ale ne v moudrosti.

< Yobu 4 >