< Yobu 4 >
1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Tad prozbori Elifaz Temanac i reče:
2 “Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
“Možeš li podnijeti da ti progovorim? Ali tko se može uzdržat' od riječi!
3 Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
Eto, mnoge ljude ti si poučio, okrijepio si iznemogle mišice;
4 Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
riječju svojom klonule si pridizao, ojačavao si koljena klecava.
5 Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
A kad tebe stiže, klonuo si duhom, na tebe kad pade, čitav si se smeo!
6 Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
Zar pobožnost tvoja nadu ti ne daje, neporočnost tvoja životu ufanje?
7 “Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
TÓa sjeti se: nevin - propade li kada? Kada su zatrti bili pravednici?
8 Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
Iz iskustva zborim: nesrećom tko ore i nevolju sije, nju će i požeti.
9 Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
Od daha Božjega oni pogibaju, na gnjevni mu disaj nestaju sa zemlje.
10 Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
Rika lavlja, urlik leopardov krše se k'o zubi u lavića.
11 Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
Lav ugiba jer mu nesta plijena, rasuli se mladi lavičini.
12 “Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
Tajna riječ se meni objavila, šapat njen je uho moje čulo.
13 Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
Noću, kada snovi duh obuzmu i san dubok kad na ljude pada,
14 ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
strah i trepet mene su svladali, kosti moje žestoko se stresle.
15 Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
Dah mi neki preko lica prođe, digoše se dlake na mom tijelu.
16 Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
Stajao je netko - lica mu ne poznah - ali likom bješe pred očima mojim. Posvuda tišina; uto začuh šapat:
17 ‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
'Zar je smrtnik koji pred Bogom pravedan? Zar je čovjek čist pred svojim Stvoriteljem?
18 Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
Ni slugama svojim više ne vjeruje, i anđele svoje za grijeh okrivljuje -
19 nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
kako ne bi onda goste stanova glinenih kojima je temelj u prahu zemaljskom. Gle, kao moljce njih sveudilj satiru:
20 Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
od jutra do mraka u prah pretvore, nestaju zasvagda - nitko i ne vidi.
21 Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’
Iščupan je kolčić njihova šatora, pogibaju skoro, mudrost ne spoznavši.'