< Yobu 4 >
1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Тогава теманецът Елифаз проговаряйки рече:
2 “Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
Ако започнем да ти говорим, ще ти дотегне ли? Но кой може се въздържа да не говори?
3 Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
Ето, ти си научил мнозина, И немощни ръце си укрепил.
4 Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
Твоите думи са заякчили колебаещия, И отслабнали колене си укрепил.
5 Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
А сега това дойде на тебе, и ти е дотегнало; Допира те, и смутил си се.
6 Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
В страха ти от Бога не е ли твоето упование, И в правотата на пътищата ти твоята надежда?
7 “Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
Спомни си, моля, кой някога е погивал невинен, Или где са били изтребени праведните.
8 Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
До колко съм аз видял, ония, които орат беззаконие, И сеят нечестие, това и жънат.
9 Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
Изтребват се от дишането на Бога, И от духането на ноздрите Му погиват.
10 Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
Ревът на лъва и гласът на свирепия лъв замират, И зъбите на младите лъвове се изкъртват.
11 Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
Лъвът загива от нямане лов, И малките на лъвицата се разпръсват.
12 “Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
Тайно достига до мене едно нещо, И ухото ми долови един шепот от него:
13 Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
Всред мислите от нощните видения, Когато дълбок сън напада човеците,
14 ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
Ужас ме обзе, и трепет, И разтърси всичките ми кости;
15 Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
Тогава дух премина пред мене; Космите на тялото ми настръхнаха;
16 Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
Той застана, но не можах да позная образа му; Призрак се яви пред очите ми; В тишина чух тоя глас:
17 ‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
Ще бъде ли смъртен човек праведен пред Бога? Ще бъде ли човека чист пред Създателя си?
18 Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
Ето, Той не се доверява на слугите Си, И на ангелите Си намира недостатък,
19 nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
Колко повече в ония, които живеят в къщи от кал. Чиято основа е в пръстта, И които се смазват като че ли са молци!
20 Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
Между заранта и вечерта се събират, Без да усети някой загубват се за винаги.
21 Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’
Величието, което е в тях, не се ли премахва? Умират и то без мъдрост.