< Yobu 39 >
1 “Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
“So wunim bere a bepɔw so mmirekyi wowo? Woahwɛ, ahu bere a ɔforote nyinsɛn ne ba?
2 Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
So woakan asram dodow a wɔde nyinsɛn? Wunim bere a wɔwo ana?
3 Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
Wɔkotow wowo wɔn mma; wɔn awoko yaw to twa.
4 Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
Wɔn mma nyin ahoɔden so wɔ wuram; na wogyaw wɔn awofo hɔ a wɔnnsan nkɔ wɔn nkyɛn bio.
5 “Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
“Hena na ɔma wuram afurum fa ne ho di? Hena na ɔsan ne hama?
6 Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
Mede asase kesee maa no sɛ ne fi, ne nkyene asase tamaa sɛ nʼatenae.
7 Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
Ɔserew kurom gyegyeegyeyɛ; na ɔnte ɔkafo nteɛteɛmu.
8 Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
Okyinkyin mmepɔw no so sɛ ne didibea ɛhɔ na okyin hwehwɛ wura amono biara.
9 “Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
“Ɛko bɛpene sɛ ɔbɛsom wo ana? Ɔbɛtena wo mmoa adididaka nkyɛn anadwo ana?
10 Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
Wubetumi asa no wɔ funtumfiri so ana? Ɔbɛfɛntɛm aku a ɛda wʼakyi no ana?
11 Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
Wubetumi de wo ho ato no so esiane nʼahoɔden dodo nti? Wubegyaw wʼadwuma a ɛyɛ den no ama no ana?
12 Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
Wugye di sɛ ɔde wʼaburow bɛba na waboa ano de akɔ awiporowbea ana?
13 “Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
“Sohori bɔ ne ntaban mu anigye so, nanso wontumi mfa ntoto asukɔnkɔn de ho.
14 Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
Ɔtow ne nkesua gu asase so ma mfutuma ka no hyew,
15 nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
ɛmfa ne ho sɛ ɛnan bi bɛpɛtɛw no, sɛ wuram aboa bi betiatia so.
16 Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
Ɔbɔ ne mma atirimɔden sɛnea wɔnyɛ ne dea; ɛmfa ne ho sɛ nʼadwuma bɛyɛ ɔkwa,
17 Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
efisɛ Onyankopɔn amma no nyansa wamma no nhumu biara.
18 Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
Nanso sɛ ɔtrɛw ne ntaban mu tu mmirika a, ɔserew ɔpɔnkɔ ne ne sotefo.
19 “Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
“Wo na woma ɔpɔnkɔ no nʼahoɔden anaa woma ne kɔn mu nwi kuhaa no?
20 Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
Wo na woma no huruw te sɛ mmoadabi, na ɔde ne nkotɔ hunahuna ana?
21 Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
Ɔde ne nan tintim fam dennen, na nʼani gye nʼahoɔden mu, na afei ɔbɔ wura ɔko mu.
22 Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
Ɔmmɔ hu, na onsuro biribiara; ohu afoa a onguan.
23 Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
Bɛmma wosow wɔ ne nkyɛn mu boha mu, na peaw ne pɛmɛ nso di ahim wɔ ne ho.
24 Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
Ofi ahopere mu de nʼano sisi fam; na sɛ wɔhyɛn torobɛnto a ontumi nnyina faako.
25 Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
Sɛ torobɛnto hyɛn a ɔka se, ‘Wiɛ!’ ɔte ɔko ho hua fi akyirikyiri, ɔsahene no nteɛmu ne ɔko mu osebɔ.
26 “Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
“Wo nyansa na ɛma akoroma tu na ɔtrɛw ne ntaban mu fa anafo?
27 Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
Wo na wohyɛ ɔkɔre ma no tu kɔ sorosoro kɔyɛ ne berebuw wɔ hɔ?
28 Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
Ɔbotan mu na ɔte na ɛhɔ na ɔda; ɔbotan sorɔnsorɔn yɛ nʼabandennen.
29 Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
Ɛhɔ na ofi kɔhwehwɛ nʼaduan; nʼani hu ade a ɛwɔ akyirikyiri.
30 Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”
Mogya yɛ ne mma aduan, na faako a atɔfo wɔ no, ɛhɔ na ɔwɔ.”