< Yobu 39 >

1 “Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
Ismered-e a kőszáli zergék ellésének idejét, a szarvasünőnek vajúdását megvigyázod-e;
2 Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
számlálod-e a hónapokat, melyeket kitöltenek, s ismered-e ellésük idejét?
3 Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
Legörnyednek, kölykeiket világra hozzák, fájdalmaikat elbocsátják.
4 Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
Fiaik erőre kapnak, felnövekednek a szabadban, kimennek és nem térnek vissza.
5 “Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
Ki bocsátotta szabadon a vadszamarat, s az erdei szamár köteleit ki oldotta meg?
6 Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
Amelynek a sivatagot tettem házává, és lakásává a sós földet;
7 Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
nevet a városnak zaján, a hajtónak lármázását nem hallja;
8 Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
a mit a hegyeken kifürkészett, az legelője, s minden zöld után kutat.
9 “Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
Akarna-e a reém téged szolgálni, avagy meghál-e jászolodnál?
10 Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
Odakötöd-e a reémet istrángjával a barázdához, vagy boronálja-e a völgyeket to utánad?
11 Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
Bízhatsz-e benne, mert nagy az ereje, s ráhagyhatod-e szerzeményedet?
12 Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
Hiszel-e benne, hogy behordja vetésedet s begyűjti szérűdre?
13 “Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
A strucznak szárnya vígan csattog, vajon tolla jámbor-e, meg tollazata?
14 Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
Mert a földnek hagyja tojásait és a poron melegíti,
15 nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
s felejti, hogy a láb eltiporja s a mező vadja széttapossa;
16 Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
keménykedik fiókáival, mintha nem volnának övéi, hogy hiába a fáradalma, az nem a rettegése;
17 Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
mert Isten elfeledtette vele a bölcsséget, s nem adott neki részt az értelemben.
18 Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
A midőn a magasba szökell, neveti a lovat és lovasát.
19 “Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
Adsz-e a lónak erőt, öltesz-e nyakára sörényt?
20 Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
Ugráltatod-e mint a sáskát?
21 Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
Fenséges tüsszögése – rettenet.
22 Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
Kémlelnek a síkon, akkor örvend erejében, kivonul a fegyver elébe; nevet a félelemnek, s nem retten meg s nem hátrál meg kard elől.
23 Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
Fölötte zörög a tegez, villogó dárda és lándzsa;
24 Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
tombolva és háborogva habzsolja a földet, s nem marad helyén, a mikor hallik a harsona.
25 Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
A mint hallik a harsona, azt mondja: Haj; messziről szimatolja a csatát, a vezérek dörgedelmét és a riadást.
26 “Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
A te értelmedből repül-e fel a karvaly s terjeszti szárnyait a délnek;
27 Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
avagy parancsodra emelkedik-e a sas, midőn magasba rakja fészkét?
28 Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
Sziklán lakik és honol, sziklának fokán és hegyi várban;
29 Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
onnan kémlel eledelre, messzire tekintenek ki szemei:
30 Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”
fiókái pedig vért hörpölnek, s a hol holttetemek vannak, ott van ő.

< Yobu 39 >