< Yobu 39 >

1 “Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
"Do you know the time when the mountain goats give birth? Do you watch when the doe bears fawns?
2 Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
Can you number the months that they fulfill? Or do you know the time when they give birth?
3 Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
They bow themselves, they bring forth their young, they end their labor pains.
4 Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
Their young ones become strong. They grow up in the open field. They go forth, and do not return again.
5 “Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
"Who has set the wild donkey free? Or who has loosened the bonds of the swift donkey,
6 Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
Whose home I have made the wilderness, and the salt land his dwelling place?
7 Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
He scorns the tumult of the city, neither does he hear the shouting of the driver.
8 Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
The range of the mountains is his pasture, He searches after every green thing.
9 “Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
"Will the wild ox be content to serve you? Or will he stay by your feeding trough?
10 Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
Can you hold the wild ox in the furrow with his harness? Or will he till the valleys after you?
11 Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
Will you trust him, because his strength is great? Or will you leave to him your labor?
12 Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
Will you have faith in him, that he will bring in your grain, and gather it to your threshing floor?
13 “Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
"The wings of the ostrich wave proudly; but are they the feathers and plumage of love?
14 Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
For she leaves her eggs on the earth, warms them in the dust,
15 nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
and forgets that the foot may crush them, or that the wild animal may trample them.
16 Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
She deals harshly with her young ones, as if they were not hers. Though her labor is in vain, she is without fear,
17 Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
because God has deprived her of wisdom, neither has he imparted to her understanding.
18 Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
When she lifts up herself on high, she scorns the horse and his rider.
19 “Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
"Have you given the horse might? Have you clothed his neck with a quivering mane?
20 Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
Have you made him to leap as a locust? The glory of his snorting is awesome.
21 Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
He paws in the valley, and rejoices in his strength. He goes out to meet the armed men.
22 Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
He mocks at fear, and is not dismayed, neither does he turn back from the sword.
23 Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
The quiver rattles against him, the flashing spear and the javelin.
24 Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
He eats up the ground with fierceness and rage, neither does he stand still at the sound of the trumpet.
25 Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
As often as the trumpet sounds he snorts, 'Aha.' He smells the battle afar off, the thunder of the captains, and the shouting.
26 “Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
"Is it by your wisdom that the hawk soars, and stretches her wings toward the south?
27 Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
Is it at your command that the eagle mounts up, and makes his nest on high?
28 Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
On the cliff he dwells, and makes his home, on the point of the cliff, and the stronghold.
29 Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
From there he spies out the prey. His eyes see it afar off.
30 Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”
His young ones also suck up blood. Where the slain are, there he is."

< Yobu 39 >