< Yobu 39 >
1 “Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
“Have you known the time of The bearing of the wild goats of the rock? Do you mark the bringing forth of does?
2 Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
Do you number the months they fulfill? And have you known the time of their bringing forth?
3 Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
They bow down, They bring forth their young ones safely, They cast forth their pangs.
4 Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
Their young ones are safe, They grow up in the field, they have gone out, And have not returned to them.
5 “Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
Who has sent forth the wild donkey free? Indeed, who opened the bands of the wild donkey?
6 Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
Whose house I have made the wilderness, And his dwellings the barren land,
7 Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
He laughs at the multitude of a city, He does not hear the cries of an exactor.
8 Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
The range of mountains [is] his pasture, And he seeks after every green thing.
9 “Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
Is a wild ox willing to serve you? Does he lodge by your crib?
10 Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
Do you bind a wild ox in a furrow [with] his thick band? Does he harrow valleys after you?
11 Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
Do you trust in him because his power [is] great? And do you leave your labor to him?
12 Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
Do you trust in him That he brings back your seed, And gathers [it to] your threshing-floor?
13 “Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
[The] wing of the crying ostriches exults, but as a pinion and feather of a stork?
14 Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
For she leaves her eggs on the earth, And she warms them on the dust,
15 nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
And she forgets that a foot may press it, And a beast of the field treads it down.
16 Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
It has hardened her young ones without her, Her labor [is] in vain, without fear.
17 Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
For God has caused her to forget wisdom, And He has not given a portion To her in understanding;
18 Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
At the time she lifts herself up on high, She laughs at the horse and his rider.
19 “Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
Do you give might to the horse? Do you clothe his neck [with] a mane?
20 Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
Do you cause him to rush as a locust? The splendor of his snorting [is] terrible.
21 Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
They dig in a valley, and he rejoices in power, He goes forth to meet the armor.
22 Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
He laughs at fear, and is not frightened, And he does not turn back from the face of the sword.
23 Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
Quiver rattles against him, The flame of a spear, and a javelin.
24 Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
He swallows the ground with trembling and rage, And does not remain steadfast Because of the sound of a horn.
25 Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
Among the horns he says, Aha, And from afar he smells battle, Roaring of princes and shouting.
26 “Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
By your understanding does a hawk fly? Does he spread his wings to the south?
27 Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
At your command does an eagle go up high? Or lift up his nest?
28 Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
He inhabits a rock, Indeed, he lodges on the tooth of a rock, and fortress.
29 Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
From there he has sought food, His eyes look attentively to a far-off place,
30 Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”
And his brood sucks up blood, And where the pierced [are]—there [is] he!”