< Yobu 39 >

1 “Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
[Say] if you know the time of the bringing forth of the wild goats of the rock, and [if] you have marked the calving of the hinds:
2 Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
and [if] you has have numbered the full months of their being with young, and [if] you have relieved their pangs:
3 Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
and have reared their young without fear; and will you loosen their pangs?
4 Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
Their young will break forth; they will be multiplied with offspring: [their young] will go forth, and will not return to them.
5 “Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
And who is he that sent forth the wild ass free? and who loosed his bands?
6 Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
whereas I made his habitation the wilderness, and the salt land his coverts.
7 Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
He laughs to scorn the multitude of the city, and hears not the chiding of the tax-gatherer.
8 Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
He will survey the mountains [as] his pasture, and he seeks after every green thing.
9 “Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
And will the unicorn be willing to serve you, or to lie down at your manger?
10 Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
And will you bind his yoke with thongs, or will he plow furrows for you in the plain?
11 Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
And do you trust him, because his strength is great? and will you commit your works to him?
12 Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
And will you believe that he will return to you your seed, and bring [it] in [to] your threshing floor?
13 “Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
The peacock has a beautiful wing: if the stork and the ostrich conceive, [it is worthy of notice],
14 Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
for [the ostrich] will leave her eggs in the ground, and warm them on the dust,
15 nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
and has forgotten that the foot will scatter them, and the wild beasts of the field trample them.
16 Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
She has hardened [herself] against her young ones, as though [she bereaved] not herself: she labors in vain without fear.
17 Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
For God has withholden wisdom from her, and not given her a portion in understanding.
18 Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
In her season she will lift herself on high; she will scorn the horse and his rider.
19 “Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
Hast you invested the horse with strength, and clothed his neck with terror?
20 Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
And have you clad him in perfect armor, and made his breast glorious with courage?
21 Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
He paws exulting in the plain, and goes forth in strength into the plain.
22 Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
He laughs to scorn a king as he meets him, and will by no means turn back from the sword.
23 Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
The bow and sword resound against him; and [his] rage will swallow up the ground:
24 Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
and he will not believe until the trumpet sounds.
25 Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
And when the trumpet sounds, he says, Aha! and afar off he smells the war with prancing and neighing.
26 “Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
And does the hawk remain steady by your wisdom, having spread out her wings unmoved, looking toward the region of the south?
27 Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
And does the eagle rise at your command, and the vulture remain sitting over his nest,
28 Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
on a crag of a rock, and in a secret [place]?
29 Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
Thence he seeks food, his eyes observe from far.
30 Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”
And his young ones roll themselves in blood, and wherever the carcasses may be, immediately they are found.

< Yobu 39 >