< Yobu 39 >
1 “Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
Kender du Tiden, da Stengeden føder, tager du Vare på Hindenes Veer,
2 Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
tæller du mon deres Drægtigheds Måneder, kender du Tiden, de føder?
3 Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
De lægger sig ned og føder og kaster Kuldet,
4 Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
Ungerne trives, gror til i det frie, løber bort og kommer ej til dem igen.
5 “Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
Hvem slap Vildæslet løs, hvem løste mon Steppeæslets Reb,
6 Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
som jeg gav Ørkenen til Hjem, den salte Steppe til Bolig?
7 Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
Det ler ad Byens Larm og hører ej Driverens Skælden;
8 Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
det ransager Bjerge, der har det sin Græsgang, det leder hvert Græsstrå op.
9 “Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
Er Vildoksen villig at trælle for dig, vil den stå ved din Krybbe om Natten?
10 Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
Binder du Reb om dens Hals, pløjer den Furerne efter dig?
11 Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
Stoler du på dens store Kræfter; overlader du den din Høst?
12 Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
Tror du, den kommer tilbage og samler din Sæd på Loen?
13 “Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
Mon Strudsens Vinge er lam, eller mangler den Dækfjer og Dun,
14 Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
siden den betror sine Æg til Jorden og lader dem varmes i Sandet,
15 nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
tænker ej på, at en Fod kan knuse dem, Vildtet på Marken træde dem sønder?
16 Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
Hård ved Ungerne er den, som var de ej dens; spildt er dens Møje, det ængster den ikke.
17 Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
Thi Gud lod den glemme Visdom og gav den ej Del i Indsigt.
18 Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
Når Skytterne kommer, farer den bort, den ler ad Hest og Rytter.
19 “Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
Giver du Hesten Styrke, klæder dens Hals med Manke
20 Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
og lærer den Græshoppens Spring? Dens stolte Prusten indgyder Rædsel.
21 Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
Den skraber muntert i Dalen, går Brynjen væligt i Møde;
22 Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
den ler ad Rædselen, frygter ikke og viger ikke for Sværdet;
23 Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
Koggeret klirrer over den, Spydet og Køllen blinker;
24 Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
den sluger Vejen med gungrende Vildskab, den tøjler sig ikke, når Hornet lyder;
25 Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
et Stød i Hornet, straks siger den: Huj! Den vejrer Kamp i det fjerne, Kampskrig og Førernes Råb.
26 “Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
Skyldes det Indsigt hos dig, at Falken svinger sig op og breder sin Vinge mod Sønden?
27 Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
Skyldes det Bud fra dig, at Ørnen flyver højt og bygger sin højtsatte Rede?
28 Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
Den bygger og bor på Klipper, på Klippens Tinde og Borg;
29 Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
den spejder derfra efter Æde, viden om skuer dens Øjne.
30 Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”
Ungerne svælger i Blod; hvor Valen findes, der er den!