< Yobu 39 >
1 “Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
Знаеш ли времето, когато раждат дивите кози по канарите? Забелязваш ли кога раждат кошутите?
2 Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
Преброяваш ли колко месеци изпълняват те? Или знаеш ли срока за раждането им?
3 Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
Когато се навеждат, раждат малките си, Освобождават се от болките си.
4 Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
Малките им заякват, растат в полето; Излизат и не се връщат вече при тях.
5 “Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
Кой е пуснал на свобода дивия осел? Или кой е развързал връзките на тоя плах бежанец,
6 Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
За кой съм направил пустинята за къща И солената земя за негово жилище?
7 Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
Той се присмива на градския шум, Нито внимава на викането на този, който го кара.
8 Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
Планините, които обикаля, са пасбището му; И търси всякаква зеленина.
9 “Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
Ще благоволи ли дивият вол да ти работи, Или ще нощува ли в твоите ясли?
10 Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
Можеш ли да впрегнеш дивия вол за оране? Или ще браносва ли той полетата зад тебе?
11 Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
Ще се облегнеш ли на него, защото силата му е голяма? Или ще повериш ли на него работата си?
12 Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
Ще се довериш ли на него да ти прибере житото ти И да го събере в гумното ти?
13 “Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
Крилата на камилоптицата пляскат весело; Но крилата и перата й благи ли са?
14 Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
Защото тя оставя яйцата си на земята И ги топли в пръстта,
15 nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
А забравя, че е възможно нога да ги смаже Или полски звяр да ги стъпче.
16 Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
Носи се жестоко с малките си, като че не са нейни; Трудът й е напразно, защото не я е грижа за опасности:
17 Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
Понеже Бог я е лишил от мъдрост, И не я е обдарил с разум.
18 Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
Когато стане да бяга Присмива се на коня и на ездача му.
19 “Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
Ти ли си дал сила на коня? Облякъл си врата му с трептяща грива?
20 Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
Ти ли го правиш да скача като скакалец? Гордото му пръхтене е ужасно.
21 Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
Копае с крак в долината, и се радва на силата си; Излиза срещу оръжията.
22 Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
Присмива се на страха и не се бои. Нито се обръща назад от меча,
23 Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
Тула по страната му трещи, И лъскавото копие, и сулицата.
24 Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
С буйство и ярост той гълта земята; И при гласа на тръбата не вярва от радост.
25 Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
Щом свири тръбата, той казва: Хо, хо! И от далеч подушва боя, Гърменето на военачалниците и викането.
26 “Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
Чрез твоята ли мъдрост лети на горе ястребът, И простира крилата си към юг?
27 Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
При твоята ли заповед се възвишава орелът, И при гнездото си по височините?
28 Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
Живее по канарите, и там се помещава, По върховете на скалите, и по непроходимите места.
29 Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
От там си съзира плячка, Очите му я съглеждат от далеч.
30 Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”
И пилетата му смучат кръв; И дето има трупове, там е той.