< Yobu 38 >

1 Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
Kisha Bwana akamjibu Ayubu kutoka upepo wa kisulisuli. Akasema:
2 “Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
“Nani huyu atiaye mashauri yangu giza kwa maneno yasiyo na maarifa?
3 Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
Jikaze kama mwanaume; nitakuuliza swali, nawe unijibu.
4 “Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
“Ulikuwa wapi nilipoweka misingi ya dunia? Niambie, kama unafahamu.
5 Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
Ni nani aliyeweka alama vipimo vyake? Hakika wewe unajua! Ni nani aliyenyoosha kamba ya kupimia juu yake?
6 Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
Je, misingi yake iliwekwa juu ya nini, au ni nani aliyeweka jiwe la pembeni,
7 pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
wakati nyota za asubuhi zilipoimba pamoja, na malaika wote walipokuwa wakipiga kelele kwa furaha?
8 “Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
“Ni nani aliyeifungia bahari milango ilipopasuka kutoka tumbo,
9 pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
nilipoyafanya mawingu kuwa vazi lake, na kuyafungia katika giza nene,
10 pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
nilipoamuru mipaka yake, na kuiweka milango yake na makomeo mahali pake,
11 Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
niliposema, ‘Unaweza kufika mpaka hapa wala si zaidi; hapa ndipo mawimbi yako yenye kiburi yatakapokomea’?
12 “Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
“Umepata kuiamrisha asubuhi ipambazuke, au kuyaonyesha mapambazuko mahali pake,
13 kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
yapate kushika miisho ya dunia, na kuwakungʼuta waovu waliomo?
14 Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
Dunia hubadilika kama udongo wa mfinyanzi chini ya lakiri; sura yake hukaa kama ile ya vazi.
15 Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
Waovu huzuiliwa nuru yao, nao mkono wao ulioinuliwa huvunjwa.
16 “Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
“Je, umepata kufika kwenye chemchemi za bahari? Au kutembea mahali pa ndani pa vilindi?
17 Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
Umewahi kuonyeshwa malango ya mauti? Umewahi kuiona milango ya uvuli wa mauti?
18 Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
Je, wewe unafahamu ukubwa wa dunia? Niambie kama unajua haya yote.
19 “Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
“Njia ya kufika kwenye makao ya nuru ni ipi? Nako maskani mwa giza ni wapi?
20 Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
Je, unaweza kuvirudisha kwenye makao yake? Unajua njia za kufika maskani mwake?
21 Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
Hakika unajua, kwa kuwa ulikuwa umeshazaliwa! Kwani umeishi miaka mingi!
22 “Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
“Je, umeshawahi kuingia katika ghala za theluji, au kuona ghala za mvua ya mawe,
23 zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
ambazo nimeziweka akiba kwa ajili ya wakati wa taabu, na kwa ajili ya wakati wa vita na mapigano?
24 Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
Ni ipi njia iendayo mahali umeme wa radi unapotawanyiwa, au mahali upepo wa mashariki unaposambaziwa juu ya dunia?
25 Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
Ni nani aliyepasua mifereji kwa ajili ya maji mengi ya mvua yaendayo kasi na njia ya umeme wa radi,
26 kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
ili kusababisha mvua kunyeshea mahali pasipokaliwa na mtu, jangwa lisilo na yeyote ndani yake,
27 kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
ili kuitosheleza nchi ya ukiwa na jangwa, na majani yaanze kumea ndani yake?
28 Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
Je, mvua ina baba? Ni nani baba azaaye matone ya umande?
29 Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
Barafu inatoka tumbo la nani? Ni nani azaaye ukungu kutoka mbinguni,
30 pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
wakati maji yawapo magumu kama jiwe, wakati uso wa vilindi vya maji unapoganda?
31 “Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
“Je, waweza kuufunga mnyororo wa Kilimia? Waweza kulegeza kamba za Orioni?
32 Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
Waweza kuyaongoza makundi ya nyota kwa majira yake, au kuongoza Dubu na watoto wake?
33 Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
Je, unajua sheria zinazotawala mbingu? Waweza kuweka utawala wa Mungu duniani?
34 “Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
“Waweza kuiinua sauti yako mpaka mawinguni, na kujifunika mwenyewe na gharika ya maji?
35 Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
Je, wewe hutuma umeme wa radi kwenye njia zake? Je, hutoa taarifa kwako kukuambia, ‘Sisi tuko hapa’?
36 Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
Ni nani aliyeujalia moyo hekima au kuzipa akili ufahamu?
37 Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
Nani mwenye hekima ya kuyahesabu mawingu? Ni nani awezaye kuinamisha magudulia ya mbinguni
38 pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
wakati mavumbi yawapo magumu, na mabonge ya udongo kushikamana pamoja?
39 “Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
“Je, utamwindia simba jike mawindo, na kuwashibisha simba wenye njaa
40 pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
wakati wao wamejikunyata mapangoni mwao, au wakivizia kichakani?
41 Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?
Ni nani ampaye kunguru chakula wakati makinda yake yanamlilia Mungu, yakizungukazunguka kwa ajili ya kukosa chakula?

< Yobu 38 >