< Yobu 38 >
1 Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
Y RESPONDIÓ Jehová á Job desde un torbellino, y dijo:
2 “Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
¿Quién es ése que oscurece el consejo con palabras sin sabiduría?
3 Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
Ahora ciñe como varón tus lomos; yo te preguntaré, y hazme saber tú.
4 “Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
¿Dónde estabas cuando yo fundaba la tierra? házme[lo] saber, si tienes inteligencia.
5 Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
¿Quién ordenó sus medidas, si lo sabes? ¿ó quién extendió sobre ella cordel?
6 Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
¿Sobre qué están fundadas sus basas? ¿ó quién puso su piedra angular,
7 pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
Cuando las estrellas todas del alba alababan, y se regocijaban todos los hijos de Dios?
8 “Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
¿Quién encerró con puertas la mar, cuando se derramaba por fuera [como] saliendo de madre;
9 pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
Cuando puse yo nubes por vestidura suya, y por su faja oscuridad.
10 pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
Y establecí sobre ella mi decreto, y le puse puertas y cerrojo,
11 Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
Y dije: Hasta aquí vendrás, y no pasarás adelante, y ahí parará la hinchazón de tus ondas?
12 “Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
¿Has tú mandado á la mañana en tus días? ¿has mostrado al alba su lugar,
13 kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
Para que ocupe los fines de la tierra, y que sean sacudidos de ella los impíos?
14 Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
Trasmúdase como lodo bajo de sello, y viene á estar como [con] vestidura:
15 Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
Mas la luz de los impíos es quitada de ellos, y el brazo enaltecido es quebrantado.
16 “Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
¿Has entrado tú hasta los profundos de la mar, y has andado escudriñando el abismo?
17 Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
¿Hante sido descubiertas las puertas de la muerte, y has visto las puertas de la sombra de muerte?
18 Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
¿Has tú considerado hasta las anchuras de la tierra? Declara si sabes todo esto.
19 “Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
¿Por dónde va el camino á la habitación de la luz, y dónde está el lugar de las tinieblas?
20 Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
¿Si llevarás tú [ambas cosas] á sus términos, y entenderás las sendas de su casa?
21 Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
¿Sabíaslo tú porque hubieses ya nacido, ó [porque es] grande el número de tus días?
22 “Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
¿Has tú entrado en los tesoros de la nieve, ó has visto los tesoros del granizo,
23 zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
Lo cual tengo yo reservado para el tiempo de angustia, para el día de la guerra y de la batalla?
24 Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
¿Por qué camino se reparte la luz, y se esparce el viento solano sobre la tierra?
25 Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
¿Quién repartió conducto al turbión, y camino á los relámpagos y truenos,
26 kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
Haciendo llover sobre la tierra deshabitada, sobre el desierto, donde no hay hombre,
27 kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
Para hartar la [tierra] desierta é inculta, y para hacer brotar la tierna hierba?
28 Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
¿Tiene la lluvia padre? ¿ó quién engendró las gotas del rocío?
29 Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
¿De qué vientre salió el hielo? y la escarcha del cielo, ¿quién la engendró?
30 pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
Las aguas se endurecen á manera de piedra, y congélase la haz del abismo.
31 “Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
¿Podrás tú impedir las delicias de las Pléyades, ó desatarás las ligaduras del Orión?
32 Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
¿Sacarás tú á su tiempo los signos de los cielos, ó guiarás el Arcturo con sus hijos?
33 Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
¿Supiste tú las ordenanzas de los cielos? ¿dispondrás tú de su potestad en la tierra?
34 “Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
¿Alzarás tú á las nubes tu voz, para que te cubra muchedumbre de aguas?
35 Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
¿Enviarás tú los relámpagos, para que ellos vayan? ¿y diránte ellos: Henos aquí?
36 Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
¿Quién puso la sabiduría en el interior? ¿ó quién dió al entendimiento la inteligencia?
37 Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
¿Quién puso por cuenta los cielos con sabiduría? y los odres de los cielos, ¿quién los hace parar,
38 pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
Cuando el polvo se ha convertido en dureza, y los terrones se han pegado unos con otros?
39 “Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
¿CAZARÁS tú la presa para el león? ¿y saciarás el hambre de los leoncillos,
40 pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
Cuando están echados en las cuevas, ó se están en sus guaridas para acechar?
41 Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?
¿Quién preparó al cuervo su alimento, cuando sus pollos claman á Dios, bullendo de un lado á otro por carecer de comida?