< Yobu 38 >

1 Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
INkosi yasimphendula uJobe isesivunguzaneni yathi:
2 “Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
Ngubani lo ofiphaza iseluleko ngamazwi angelalwazi?
3 Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
Bopha-ke ukhalo lwakho njengendoda, njalo ngizakubuza, njalo ungenze ngazi.
4 “Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
Wawungaphi lapho ngimisa izisekelo zomhlaba? Tshono uba usazi ukuqedisisa.
5 Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
Ngubani owabeka izilinganiso zawo, uba ukwazi? Kumbe ngubani owelulela intambo yokulinganisa phezu kwawo?
6 Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
Izisekelo zawo zamiswa phezu kwani? Kumbe ngubani owabeka ilitshe lawo lengonsi,
7 pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
lapho inkanyezi zokusa zahlabela kanyekanye, lamadodana wonke kaNkulunkulu amemeza ngenjabulo?
8 “Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
Kumbe ngubani owavalela ulwandle ngezivalo, lapho lufohla luphuma esiswini,
9 pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
lapho ngimisa iyezi laba yisembatho salo, lomnyama onzima waba yimbeleko yalo?
10 pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
Njalo ngaluqumela isimiso, ngamisa imigoqo lezivalo,
11 Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
ngathi: Uzafika kuze kube lapha, kodwa ungedluli, lalapha kuzamelana lokuzigqaja kwamagagasi akho.
12 “Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
Kusukela ensukwini zakho walawula ukusa yini, wenza ukudabuka kokusa ukuthi kwazi indawo yakho,
13 kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
ukuthi kubambe imiphetho yomhlaba, ukuze kuthintithe ababi kuwo?
14 Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
Kuyaguquka njengebumba lophawu lokunamathisela, kuzimisa njengesembatho.
15 Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
Lakwababi ukukhanya kwabo kuyagodlwa, lengalo ephakemeyo iyephulwa.
16 “Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
Usungenile emithonjeni yolwandle yini, wahamba usiya le lale ekudingeni inziki?
17 Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
Amasango okufa wawembulelwa yini, wawabona amasango ethunzi lokufa?
18 Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
Uqedisisile yini kuze kube sebubanzini bomhlaba? Tshono uba ukwazi konke.
19 “Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
Ingaphi indlela lapho okuhlala khona ukukhanya? Lomnyama, ingaphi indawo yawo,
20 Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
ukuze ukuse emngceleni wakho, lokuthi uqedisise izindlela zomuzi wakho?
21 Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
Uyazi, ngoba wawusuzelwe, lenani lensuku zakho likhulu.
22 “Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
Usungenile eziphaleni zeliqhwa elikhithikileyo yini, wabona iziphala zesiqhotho,
23 zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
engizigodle kuze kube yisikhathi sokuhlupheka, kuze kube lusuku lokulwa lolwempi?
24 Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
Ingaphi indlela lapho ukukhanya okwabiwa khona, umoya wempumalanga ohlakazeka khona emhlabeni?
25 Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
Ngubani owehlukanisela impophoma indlela yamanzi, lendlela yombane wemidumo,
26 kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
ukuthi line emhlabeni lapho okungelamuntu khona, enkangala okungelamuntu kuyo,
27 kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
ukusuthisa inkangala legwadule, lokuhlumisa ukuphuma kotshani?
28 Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
Izulu liloyise yini, kumbe ngubani owazala amathonsi amazolo?
29 Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
Ungqwaqwane waphuma esiswini sikabani? Njalo ngubani owazala iliqhwa lamazulu?
30 pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
Amanzi afihlakele njengelitshe, lobuso bokujula bujiyile.
31 “Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
Ungazibopha yini izibopho zesiLimela, kumbe uthukulule intambo zeziNja?
32 Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
Ungakhupha yini izinkanyezi ngesikhathi sazo? Ungakhokhela yini iBhere kanye labantwana balo?
33 Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
Uyazazi yini izimiso zamazulu, kumbe ungamisa umbuso wazo emhlabeni?
34 “Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
Ungaphakamisela yini ilizwi lakho emayezini, ukuthi ubunengi bamanzi bukusibekele?
35 Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
Ungathuma yini imibane ukuthi ihambe, ithi kuwe: Khangela, silapha?
36 Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
Ngubani owabeka inhlakanipho emibilini? Kumbe ngubani onike ukuqedisisa engqondweni?
37 Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
Ngubani ongabala amayezi ngenhlakanipho? Njalo ngubani ongalalisa imbodlela zamazulu,
38 pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
lapho uthuli luqina lube yizigaqa, lamagade anamathelane?
39 “Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
Ungasizingelela yini isilwane ukudla, kumbe usuthise ukulamba kwezilwane ezintsha,
40 pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
lapho zicathame emihomeni, zihlala esikhundleni ukuthi zicathame?
41 Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?
Ngubani olungisela iwabayi ukudla kwalo, lapho amaphuphu alo ekhala kuNkulunkulu, ezulazula ngoba kungelakudla?

< Yobu 38 >