< Yobu 38 >

1 Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
UThixo wasekhuluma loJobe ephakathi kwesiphepho. Wathi:
2 “Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
“Ngubani na lowo odunga amacebo ami ngamazwi okungazi?
3 Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
Qina njengendoda; ngizakubuza, lawe uzangiphendula.
4 “Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
Wawungaphi lapho ngibeka izisekelo zomhlaba na? Ngitshela nxa uqedisisa.
5 Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
Ngubani owamisa izilinganiso zawo na? Phela angithi uyazi! Ngubani owayidonsayo intambo yokulinganisa kuwo na?
6 Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
Izinsika zawo zamiswa phezu kwani na, loba ngubani owamisa ilitshe lawo lekhoneni na
7 pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
lapho izinkanyezi zokusa zazihlabelela kanyekanye lezingilosi zonke zamemeza ngentokozo?
8 “Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
Ngubani owavalela ulwandle ngemva kwezivalo lapho selufohla esiswini na,
9 pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
lapho ngisenza amayezi aba yisembatho salo na ngalugoqela ngomnyama omkhulu,
10 pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
lapho ngalubekela imikhawulo ngamisa iminyango yalo lemigoqo endaweni yayo,
11 Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
lapho engathi, ‘Ungeza uze ufike lapha kodwa ungedluli; kulapha amagagasi akho azigqajayo aphelela khona?’
12 “Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
Sewake wabekela ikuseni umthetho na, loba watshengisa ukusa indawo yakho
13 kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
ukuba kuphakamise umhlaba ngemiphetho kuthintithe ababi abakuwo?
14 Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
Umhlaba ubumbeka isimo njengebumba ufakwe uphawu; imibala yawo ikhanye ithi bha njengelembu.
15 Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
Ababi bayacitshelwa ukukhanya, lengalo yabo ephakanyisiweyo iyephulwa.
16 “Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
Sewake wahamba emithonjeni yolwandle na loba wahamba ezingoxweni zenziki yalo na?
17 Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
Amasango okufa aseke abonakaliswa kuwe na? Usuke wawabona amasango ethunzi lokufa na?
18 Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
Ubuqedisisile na ubukhulu bobubanzi bomhlaba? Ngitshela nxa ukwazi konke lokhu.
19 “Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
Yiphi indlela eya ekhaya elihlala ukukhanya na? Ubumnyama bona buhlala ngaphi?
20 Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
Ungakusa ezindaweni zakho na? Uyazazi izindlela eziya emizini yazo na?
21 Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
Ye uyakwazi, ngoba wawuvele usuzelwe! Usuphile iminyaka yonke le!
22 “Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
Sewake wangena eziphaleni zikangqwaqwane loba wabona iziphala zesiqhotho na,
23 zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
engizilindisele izikhathi zohlupho, insuku zempi lokuhlasela na?
24 Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
Ingaphi indlela eya esigodlweni sokwaba umbane, loba indawo yokuhlakaza umoya wempumalanga phezu komhlaba na?
25 Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
Ngubani ogubhe intshukuntshu yezihlambo zezulu, lendlela yomdumo wesiphepho;
26 kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
ukuthelezela ilizwe elingahlali muntu, inkangala okungelamuntu kuyo,
27 kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
ukusuthisa ilizwe elilugwadule kulenze lihlume utshani na?
28 Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
Izulu elinayo liloyise na? Ngubani onguyise wamathonsi amazolo na?
29 Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
Ngesikabani isisu esizala iliqhwa na? Ngubani ozala umtshazo ovela phezulu na
30 pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
lapho amanzi abalukhuni njengelitshe, lapho iphezulu yolwandle ijiyile?
31 “Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
Ungasibopha na isiLimela lesi esihle? Ungazithukulula yini izintambo zeziNja?
32 Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
Ungawuletha na uMthala ngesikhathi sawo loba ukhuphe inkanyezi ethiwa yiNgulube lemidlwane yayo?
33 Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
Uyayazi imithetho yasezulwini na? Ungawakha yini umbuso kaNkulunkulu emhlabeni?
34 “Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
Ungawamemeza yini amayezi uthi akunethise ngesihlambo samanzi?
35 Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
Uyakuthuma yini ukuphazima kombane? Uyabika kuwe yini uthi, ‘Ngilapha’?
36 Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
Ngubani owapha inhliziyo ukuhlakanipha kumbe owapha ingqondo ukuzwisisa na?
37 Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
Ngubani ololwazi lokubala amayezi na? Ngubani ongagenqula amaqhaga asezulwini na
38 pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
nxa uthuli seluqina lamagade omhlabathi esebumbene?
39 “Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
Uyasizingelela na isilwanekazi ukudla kwaso, uyiqede indlala yezilwane
40 pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
lapho zilele ezikhundleni zazo kumbe zicwathile ezixukwini?
41 Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?
Ngubani opha iwabayi ukudla lapho amatsiyane alo ekhala kuNkulunkulu ezulazula ehayila ngendlala na?”

< Yobu 38 >