< Yobu 38 >
1 Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
Tad Tas Kungs Ījabam atbildēja no vētras un sacīja:
2 “Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
Kas tas tāds, kas (Dieva) padomu aptumšo ar neprātīgiem vārdiem?
3 Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
Apjoz jel kā vīrs savus gurnus, tad Es tev gribu vaicāt, un tu Mani māci.
4 “Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
Kur tu biji, kad Es zemei liku pamatu? Izteic to, ja tev ir tāds gudrs prāts.
5 Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
Vai tu zini, kas viņai mēru licis, jeb kas pār viņu ir vilcis mēra auklu?
6 Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
Uz ko viņas pamati ierakti, jeb kas licis viņas stūra akmeni,
7 pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
Kad rīta zvaigznes kopā priecīgi dziedāja, un visi Dieva bērni gavilēja?
8 “Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
Jeb kas jūru aizslēdzis ar durvīm, kad tā izlauzās, un iznāca kā no mātes miesām,
9 pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
Kad Es to ģērbu ar padebešiem, un krēslībā ietinu tā kā tinamos autos,
10 pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
Kad Es tai noliku Savu robežu, un liku aizšaujamos un durvis,
11 Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
Un sacīju: tiktāl tev būs nākt un ne tālāki, un še būs apgulties taviem lepniem viļņiem?
12 “Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
Vai tu savā mūžā rītam licis aust, vai auseklim rādījis savu vietu,
13 kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
Lai satver zemes stūrus, ka tie bezdievīgie no tās top izkratīti;
14 Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
Ka tā pārvēršas kā zieģeļa vasks un visas lietas rādās kā apģērbā,
15 Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
Un bezdievīgiem zūd viņu gaišums, un pacelts elkonis salūst?
16 “Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
Vai tu esi nācis līdz jūras avotam un staigājis bezdibeņu dziļumos?
17 Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
Vai tev atdarījušies nāves vārti, un vai tu esi redzējis nāves ēnas vārtus?
18 Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
Vai esi skatījies līdz pasaules malām? Stāsti, ja tu visu to zini.
19 “Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
Kur ir tas ceļš, kur gaisma mājo, un tumsa - kur ir viņas vieta?
20 Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
Vai tu to varētu pārvest viņas robežā un izzināt viņas nama ceļus?
21 Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
Tu to zini, jo tai laikā tu biji piedzimis, un tev ir daudz to gadu!
22 “Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
Vai tu esi nācis, kur tie sniega krājumi, un vai esi redzējis krusas krājumus,
23 zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
Ko Es taupu uz spaidu laiku, uz kaušanas un kara dienu?
24 Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
Pa kuru ceļu gaisma dalās un kā austrenis izplešas virs zemes?
25 Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
Kas lietum rādījis, kur lai gāžas, un ceļu zibeņiem un pērkoniem,
26 kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
Ka lietus līst, kur cilvēka nav, tuksnesī, kur neviens nedzīvo,
27 kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
Ka viņš dzirdina tukšo posta vietu un zālītei liek dīgt?
28 Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
Vai lietum ir tēvs, vai kas dzemdinājis rasas lāsi?
29 Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
No kura klēpja cēlies ledus, un no kā dzimusi debess salna,
30 pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
Ka ūdeņi sastingst kā akmens, un jūras dziļumi aizsalst cieti?
31 “Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
Vai tu vari sasiet Sietiņa saites, vai atraisīt Orijona zvaigžņu saiti?
32 Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
Vai tu zvaigznes vari izvest savā laikā un vadīt debess vāģus un viņu ratus?
33 Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
Vai tu zini debess likumus, jeb vai proti, kā tie valda virs zemes?
34 “Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
Vai tu savu balsi vari pacelt uz padebešiem, lai ūdeņi plūst zemē uz tevi?
35 Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
Vai vari sūtīt zibeņus, ka tie iet un uz tevi saka: redzi, še mēs esam?
36 Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
Kas lika gudrību tumšos mākoņos un prātu debess spīdumos?
37 Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
Kas skaita mākoņus ar gudrību, un kas māk apgāzt padebešus,
38 pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
Ka pīšļi top aplieti, ka tie saskrien un salīp pītēs?
39 “Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
Vai tu māki medīt laupījumu priekš lauvas un pildīt jauno lauvu tukšo vēderu,
40 pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
Kad tie nogulstas alās un biezos krūmos glūn?
41 Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?
Kas gādā krauklim barību, kad viņa bērni uz Dievu brēc un šurpu turpu skraida, kad nav ko ēst?