< Yobu 38 >
1 Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
Alors l'Eternel répondit à Job du milieu d'un tourbillon, et lui dit:
2 “Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
Qui est celui-ci qui obscurcit le conseil par des paroles sans science?
3 Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
Ceins maintenant tes reins comme un vaillant homme, et je t'interrogerai, et tu me feras voir quelle est ta science.
4 “Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
Où étais-tu quand je fondais la terre? dis-le-moi, si tu as de l'intelligence.
5 Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
Qui est-ce qui en a réglé les mesures? le sais-tu? ou qui est-ce qui a appliqué le niveau sur elle?
6 Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
Sur quoi sont plantés ses pilotis, ou qui est celui qui a posé la pierre angulaire pour la soutenir.
7 pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
Quand les étoiles du matin se réjouissaient ensemble, et que les fils de Dieu chantaient en triomphe?
8 “Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
Qui est-ce qui a renfermé la mer dans ses bords, quand elle fut tirée de la matrice, [et] qu'elle en sortit?
9 pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
Quand je mis la nuée pour sa couverture, et l'obscurité pour ses langes?
10 pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
Et que j'établis sur elle mon ordonnance, et lui mis des barrières et des portes?
11 Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
Et lui dis: Tu viendras jusque là, et tu ne passeras point plus avant, et ici s'arrêtera l'élévation de tes ondes.
12 “Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
As-tu, depuis que tu es au monde, commandé au point du jour; et as-tu montré à l'aube du jour le lieu où elle doit se lever?
13 kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
Afin qu'elle saisisse les extrémités de la terre, et que les méchants se retirent à l'écart,
14 Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
Et qu'elle prenne une nouvelle forme, comme une argile figurée; et que [toutes choses y] paraissent comme avec de [nouveaux] habits,
15 Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
Et que la clarté soit défendue aux méchants, et que le bras élevé soit rompu?
16 “Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
Es-tu venu jusqu'aux gouffres de la mer, et t'es-tu promené au fond des abîmes?
17 Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
Les portes de la mort se sont-elles découvertes à toi? as-tu vu les portes de l'ombre de la mort?
18 Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
As-tu compris toute l'étendue de la terre? si tu l'as toute connue, montre-le.
19 “Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
En quel endroit se tient la lumière, et où est le lieu des ténèbres?
20 Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
Que tu ailles prendre l'une et l'autre en son quartier, et que tu saches le chemin de leur maison?
21 Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
Tu le sais; car alors tu naquis, et le nombre de tes jours est grand.
22 “Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
Es-tu entré dans les trésors de la neige? As-tu vu les trésors de la grêle,
23 zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
Laquelle je retiens pour le temps de l'affliction, et pour le jour du choc et du combat?
24 Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
Par quel chemin se partage la lumière, [et par quelle voie] le vent d'Orient se répand-il sur la terre?
25 Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
Qui est-ce qui a ouvert les conduits aux inondations, et le chemin à l'éclair des tonnerres,
26 kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
Pour faire pleuvoir sur une terre où il n'y a personne, et sur le désert où il ne demeure aucun homme.
27 kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
Pour arroser abondamment les lieux solitaires et déserts, et pour faire pousser le germe de l'herbe?
28 Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
La pluie n'a-t-elle point de père? ou qui est-ce qui produit les gouttes de la rosée?
29 Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
Du ventre de qui sort la glace? et qui est-ce qui engendre le frimas du ciel?
30 pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
Les eaux se cachent étant durcies comme une pierre, et le dessus de l'abîme se prend.
31 “Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
Pourrais-tu retenir les délices de la Poussinière, ou faire lever les tempêtes [qu'excite] la constellation d'Orion?
32 Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
Peux-tu faire lever en leur temps les signes du Zodiaque? et conduire la petite Ourse avec les étoiles?
33 Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
Connais-tu l'ordre des cieux, et disposeras-tu de leur gouvernement sur la terre?
34 “Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
Crieras-tu à haute voix à la nuée, afin qu'une abondance d'eaux t'arrose?
35 Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
Enverras-tu les foudres de sorte qu'elles partent, et te disent: Nous voici?
36 Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
Qui est-ce qui a mis la sagesse dans les reins? ou qui a donné au cœur l'intelligence?
37 Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
Qui est-ce qui a assez d'intelligence pour compter les nuées, et pour placer les outres des cieux,
38 pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
Quand la poudre est détrempée par les eaux qui l'arrosent, et que les fentes [de la terre] viennent à se rejoindre?
39 “Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
Chasseras-tu de la proie pour le vieux lion, et rassasieras-tu les lionceaux qui cherchent leur vie,
40 pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
Quand ils se tapissent dans leurs antres, et qu'ils se tiennent dans leurs forts aux aguets?
41 Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?
Qui est-ce qui apprête la nourriture au corbeau, quand ses petits crient au [Dieu] Fort, et qu'ils vont errants, parce qu'ils n'ont point de quoi manger?