< Yobu 38 >

1 Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
L’Eternel répondit à Job du sein de la tempête et dit:
2 “Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
Quel est celui qui dénigre les desseins de Dieu par des discours dépourvus de sens?
3 Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
Ceins donc tes reins comme un homme: je vais t’interroger et tu m’instruiras.
4 “Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
Où étais-tu lorsque je fondais la terre? Dis-le, si tu en as quelque connaissance.
5 Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
Qui a fixé ses dimensions, si tu le sais, ou qui a tendu sur elle le cordeau?
6 Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
Sur quoi sont assis ses piliers, ou qui a lancé sa pierre angulaire,
7 pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
tandis que les étoiles du matin chantaient en chœur, et que tous les fils de Dieu poussaient des cris de joie?
8 “Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
Qui a fermé la mer avec des portes, quand elle sortit jaillissante du sein maternel,
9 pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
quand je lui donnai la nuée pour vêtement et une brume épaisse pour langes;
10 pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
quand je brisai son élan par mes barrières et lui posai des verrous et des portes,
11 Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
et que je lui dis: "Jusqu’ici tu viendras et non au-delà: ici s’arrêtera l’orgueil de tes flots?"
12 “Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
As-tu jamais de ta vie donné des ordres au matin, assigné sa place à l’aurore,
13 kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
pour qu’elle saisisse les bords de la terre et en rejette les méchants en une secousse?
14 Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
Quand elle paraît, la terre se transforme comme l’argile sous le sceau, et les choses se présentent comme un riche vêtement.
15 Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
Les méchants sont privés de leur lumière à eux, et leur bras déjà levé est brisé.
16 “Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
As-tu pénétré jusqu’aux sources de la mer, as-tu circulé au fonds de l’abîme?
17 Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
Les portes de la mort se sont-elles dévoilées devant toi? As-tu vu l’entrée du royaume des ombres?
18 Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
As-tu mesuré l’immense étendue de la terre? Dis-le, si tu sais tout cela.
19 “Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
Quel chemin mène à la demeure de la lumière, et où est l’habitation des ténèbres,
20 Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
pour que tu les conduises dans leur domaine et reconnaisses les avenues de leur maison?
21 Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
Tu le sais sans doute! Car tu étais né dès lors, et grand est le nombre de tes jours!
22 “Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
Es-tu entré dans les trésors de la neige, as-tu aperçu les dépôts de la grêle,
23 zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
que je tiens en réserve pour les temps de détresse, pour le jour du combat et de la guerre?
24 Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
Quelle est la voie par où se disperse la lumière, par où le vent d’Est se répand sur la terre?
25 Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
Qui a creusé des rigoles à l’averse, une route à l’éclair sonore,
26 kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
pour arroser des régions inhabitées, le désert où il n’y a pas d’hommes,
27 kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
pour abreuver les terres incultes et sauvages et faire pousser l’herbe nouvelle des prairies?
28 Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
La pluie a-t-elle un père? Qui engendre les gouttes de la rosée?
29 Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
De quel sein sort la glace, et le givre du ciel, qui l’a enfanté?
30 pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
Les eaux se condensent comme la pierre et la surface des eaux se contracte.
31 “Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
Est-ce toi qui noues les bandeaux des Pléiades ou qui relâches les liens de l’Orion?
32 Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
Est-ce toi qui fais paraître les planètes en leur temps et qui diriges la Grande-Ourse avec ses petits?
33 Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
Connais-tu les lois du ciel? Est-ce toi qui règles sa force d’action sur la terre?
34 “Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
Te suffit-il d’élever ta voix vers la nuée, pour qu’elle t’envoie des masses d’eau?
35 Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
Est-ce toi qui commandes aux éclairs de partir? Te disent-ils: "Nous voici?"
36 Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
Qui a mis de la sagesse, dans la brume sombre, ou qui a donné au météore l’intelligence?
37 Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
Qui pourrait dénombrer les nuages avec sagacité, et qui incline les amphores du ciel,
38 pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
de manière à agréger la poussière en une masse compacte et à coller ensemble les glèbes de la terre?
39 “Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
Est-ce toi qui poursuis la proie pour le lion, qui assouvis la voracité des lionceaux,
40 pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
lorsqu’ils sont tapis dans leurs tanières ou se tiennent aux aguets dans les fourrés?
41 Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?
Qui prépare au corbeau sa pâture, quand ses petits crient vers Dieu et errent çà et là faute de nourriture?

< Yobu 38 >