< Yobu 38 >

1 Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
Then the LORD answered Job out of the whirlwind,
2 “Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
"Who is this who darkens counsel by words without knowledge?
3 Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
Brace yourself like a man, for I will question you, then you answer me.
4 “Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
"Where were you when I laid the foundations of the earth? Declare, if you have understanding.
5 Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
Who determined its measures, if you know? Or who stretched the line on it?
6 Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
Whereupon were its foundations fastened? Or who laid its cornerstone,
7 pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
when the morning stars sang together, and all the sons of God shouted for joy?
8 “Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
"Or who shut up the sea with doors, when it broke forth from the womb,
9 pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
when I made clouds its garment, and wrapped it in thick darkness,
10 pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
marked out for it my bound, set bars and doors,
11 Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
and said, 'Here you may come, but no further. Here your proud waves shall be stayed?'
12 “Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
"Have you commanded the morning in your days, and caused the dawn to know its place;
13 kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
that it might take hold of the farthest parts of the earth, and shake the wicked out of it?
14 Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
It is changed as clay under the seal, and stands forth as a garment.
15 Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
From the wicked, their light is withheld. The high arm is broken.
16 “Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
"Have you entered into the springs of the sea? Or have you walked in the recesses of the deep?
17 Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
Have the gates of death been revealed to you? Or have you seen the gates of the shadow of death?
18 Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
Have you comprehended the earth in its breadth? Declare, if you know it all.
19 “Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
"What is the way to the dwelling of light? As for darkness, where is its place,
20 Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
that you should take it to its bound, that you should discern the paths to its house?
21 Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
Surely you know, for you were born then, and the number of your days is great.
22 “Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
Have you entered the treasuries of the snow, or have you seen the treasures of the hail,
23 zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
which I have reserved against the time of trouble, against the day of battle and war?
24 Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
By what way is the lightning distributed, or the east wind scattered on the earth?
25 Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
Who has cut a channel for the flood water, or the path for the thunderstorm;
26 kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
To cause it to rain on a land where no man is; on the wilderness, in which there is no man;
27 kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
to satisfy the waste and desolate ground, to cause the tender grass to spring forth?
28 Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
Does the rain have a father? Or who fathers the drops of dew?
29 Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
Out of whose womb came the ice? The gray frost of the sky, who has given birth to it?
30 pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
The waters become hard like stone, when the surface of the deep is frozen.
31 “Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
"Can you fasten the chains of Kimah, or loosen the cords of Kesil?
32 Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
Can you lead forth the Mazzaroth in their season? Or can you lead Aysh with her children?
33 Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
Do you know the laws of the heavens? Can you establish its dominion over the earth?
34 “Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
"Can you lift up your voice to the clouds, That abundance of waters may cover you?
35 Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
Can you send forth lightnings, that they may go? Do they report to you, 'Here we are?'
36 Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
Who has put wisdom in the inward parts? Or who has given understanding to the mind?
37 Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
Who can number the clouds by wisdom? Or who can pour out the bottles of the sky,
38 pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
when the dust runs into a mass, and the clods of earth stick together?
39 “Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
"Can you hunt the prey for the lioness, or satisfy the appetite of the young lions,
40 pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
when they crouch in their dens, and lie in wait in the thicket?
41 Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?
Who provides for the raven his prey, when his young ones cry to God, and wander for lack of food?

< Yobu 38 >